Masalimo 65 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 65:1-13

Salimo 65

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo.

1Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni;

kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.

2Inu amene mumamva pemphero,

kwa inu anthu onse adzafika.

3Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo,

Inu munakhululukira mphulupulu zathu.

4Odala iwo amene inu muwasankha

ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu!

Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu,

za mʼNyumba yanu yoyera.

5Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo,

Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,

chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi

ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,

6amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu,

mutadziveka nokha ndi mphamvu.

7Amene munakhalitsa bata nyanja

kukokoma kwa mafunde ake,

ndi phokoso la anthu a mitundu ina.

8Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu;

kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera.

Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.

9Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira;

Inuyo mumalilemeretsa kwambiri.

Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi

kuti upereke tirigu kwa anthu,

pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.

10Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake,

mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.

11Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka,

ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.

12Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira;

mapiri avekedwa ndi chisangalalo.

13Madambo akutidwa ndi zoweta

ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu;

izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.

Het Boek

Psalmen 65:1-14

1Een psalm van David, een lied voor de koordirigent.

2U komt toe dat wij in stille verwondering

naar U opzien, o God.

Wij willen U in Jeruzalem lofliederen zingen.

Geloften willen wij U betalen.

3U hoort al onze gebeden

en alles wat leeft, mag dan ook tot U komen.

4Het kwaad dreigde mij te overmeesteren,

maar U vergeeft mij mijn zonden.

5Gelukkig is de man die U uitkiest.

U laat hem bij U komen en bij U wonen.

Al het goede van uw huis zal ons

in overvloed ten deel vallen,

al het heilige in uw tempel.

6U antwoordt ons in oprechtheid met grote daden,

God, U bevrijdt ons.

De hele aarde kan op U vertrouwen,

U bent er tot in de verste zeeën.

7Met uw kracht hebt U de bergen stevig geplant,

vastgezet door uw sterkte.

8U laat de zeeën tot kalmte komen,

zowel het bruisen van de golven

als het geschreeuw van de volken.

9Daarom zijn alle mensen,

tot in de uithoeken van de aarde,

bang voor de tekenen die U doet.

Van oost tot west brengt men U eer en lof.

10U komt naar ons toe

en geeft ons land een overvloedige oogst.

U maakt ons rijk.

De beek van God is gevuld met water.

U laat het koren groeien,

zoals U alles laat groeien.

11U geeft het water op de akkers,

doordrenkt de voren op het land.

Uw regen laat onze gewassen groeien.

U zegent de gewassen.

12Door uw goedheid wordt onze oogst bekroond,

U geeft ons overvloed.

13De rijpe gewassen golven op de akker,

de heuvels juichen over U.

14De vruchtbare streken zijn bezaaid met kudden,

in de dalen groeit welig het koren.

Heel het land jubelt en zingt.

Heel deze overvloed is er dankzij U.