Masalimo 65 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 65:1-13

Salimo 65

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo.

1Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni;

kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.

2Inu amene mumamva pemphero,

kwa inu anthu onse adzafika.

3Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo,

Inu munakhululukira mphulupulu zathu.

4Odala iwo amene inu muwasankha

ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu!

Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu,

za mʼNyumba yanu yoyera.

5Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo,

Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,

chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi

ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,

6amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu,

mutadziveka nokha ndi mphamvu.

7Amene munakhalitsa bata nyanja

kukokoma kwa mafunde ake,

ndi phokoso la anthu a mitundu ina.

8Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu;

kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera.

Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.

9Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira;

Inuyo mumalilemeretsa kwambiri.

Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi

kuti upereke tirigu kwa anthu,

pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.

10Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake,

mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.

11Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka,

ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.

12Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira;

mapiri avekedwa ndi chisangalalo.

13Madambo akutidwa ndi zoweta

ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu;

izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 65:1-13

Salmo 65

Al director musical. Salmo de David. Cántico.

1A ti, oh Dios de Sión,

te pertenece la alabanza.

A ti se te deben cumplir los votos,

2porque escuchas la oración.

A ti acude todo mortal,

3a causa de sus perversidades.

Nuestros delitos nos abruman,

pero tú los perdonaste.

4¡Dichoso aquel a quien tú escoges,

al que atraes a ti para que viva en tus atrios!

Saciémonos de los bienes de tu casa,

de los dones de tu santo templo.

5Tú, oh Dios y Salvador nuestro,

nos respondes con imponentes obras de justicia;

tú eres la esperanza de los confines de la tierra

y de los más lejanos mares.

6Tú, con tu poder, formaste las montañas,

desplegando tu potencia.

7Tú calmaste el rugido de los mares,

el estruendo de sus olas,

y el tumulto de los pueblos.

8Los que viven en remotos lugares

se asombran ante tus prodigios;

del oriente al occidente,

tú inspiras canciones de alegría.

9Con tus cuidados fecundas la tierra,

y la colmas de abundancia.

Los arroyos de Dios se llenan de agua,

para asegurarle trigo al pueblo.

¡Así preparas el campo!

10Empapas los surcos, nivelas sus terrones,

reblandeces la tierra con las lluvias

y bendices sus renuevos.

11Tú coronas el año con tus bondades,

y tus carretas se desbordan de abundancia.

12Rebosan los prados del desierto;

las colinas se visten de alegría.

13Pobladas de rebaños las praderas,

y cubiertos los valles de trigales,

cantan y lanzan voces de alegría.