Masalimo 64 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 64:1-10

Salimo 64

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga;

tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.

2Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa,

ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.

3Iwo amanola malilime awo ngati malupanga,

amaponya mawu awo olasa ngati mivi.

4Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa;

amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.

5Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa,

amayankhula zobisa misampha yawo;

ndipo amati, “Adzayiona ndani?”

6Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati,

“Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!”

Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.

7Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi;

mwadzidzidzi adzakanthidwa.

8Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa

ndi kuwasandutsa bwinja;

onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.

9Anthu onse adzachita mantha;

adzalengeza ntchito za Mulungu

ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.

10Lolani wolungama akondwere mwa Yehova

ndi kubisala mwa Iye,

owongoka mtima onse atamande Iye!

Thai New Contemporary Bible

สดุดี 64:1-10

สดุดี 64

(ถึงหัวหน้านักร้อง บทสดุดีของดาวิด)

1ข้าแต่พระเจ้า ขอทรงฟังคำร้องทุกข์ของข้าพระองค์

ขอทรงปกป้องชีวิตข้าพระองค์ให้พ้นจากการคุกคามของเหล่าศัตรู

2ขอทรงซ่อนข้าพระองค์ให้พ้นจากการสมรู้ร่วมคิดของเหล่าคนชั่ว

ให้พ้นจากอุบายของพวกคนชั่ว

3พวกเขาลับลิ้นของตนอย่างลับดาบ

และพ่นวาจาดั่งยิงธนูอาบยาพิษ

4พวกเขายิงใส่ผู้บริสุทธิ์จากที่ซุ่ม

พวกเขายิงทันทีอย่างไม่เกรงกลัว

5เขาปลุกใจซึ่งกันและกันในการวางแผนชั่ว

พวกเขาพูดกันเรื่องวางกับดักล่อเหยื่อ

เขาพูดว่า “ใครจะเห็นมัน64:5 หรือพวกเรา?”

6พวกเขาวางแผนการที่อยุติธรรมและพูดว่า

“เราได้วางแผนไว้อย่างยอดเยี่ยม!”

แน่นอน ความคิดและจิตใจของมนุษย์นั้นเจ้าเล่ห์นัก

7แต่พระเจ้าเองจะทรงยิงธนูใส่เขา

เขาจะถูกโค่นล้มโดยไม่ทันรู้ตัว

8พระองค์จะทำให้พวกเขาย่อยยับด้วยลิ้นของตนเอง

ทุกคนที่เห็นเขาจะส่ายหน้าเย้ยหยัน

9มวลมนุษยชาติจะเกรงกลัว

จะป่าวประกาศพระราชกิจของพระเจ้า

และใคร่ครวญสิ่งที่พระองค์ได้ทรงกระทำ

10ให้คนชอบธรรมชื่นชมยินดีในองค์พระผู้เป็นเจ้า

และลี้ภัยในพระองค์

ให้ผู้มีจิตใจเที่ยงธรรมสรรเสริญพระองค์เถิด!