Masalimo 64 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 64:1-10

Salimo 64

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga;

tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.

2Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa,

ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.

3Iwo amanola malilime awo ngati malupanga,

amaponya mawu awo olasa ngati mivi.

4Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa;

amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.

5Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa,

amayankhula zobisa misampha yawo;

ndipo amati, “Adzayiona ndani?”

6Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati,

“Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!”

Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.

7Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi;

mwadzidzidzi adzakanthidwa.

8Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa

ndi kuwasandutsa bwinja;

onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.

9Anthu onse adzachita mantha;

adzalengeza ntchito za Mulungu

ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.

10Lolani wolungama akondwere mwa Yehova

ndi kubisala mwa Iye,

owongoka mtima onse atamande Iye!

Nueva Versión Internacional

Salmo 64:1-10

Salmo 64Sal 64 En el texto hebreo 64:1-10 se numera 64:2-11.

Al director musical. Salmo de David.

1Escucha, oh Dios, la voz de mi queja;

protégeme del temor al enemigo.

2Escóndeme de esa pandilla de malhechores,

de esa caterva de malvados.

3Afilan su lengua como espada

y lanzan como flechas palabras ponzoñosas.

4Emboscados, disparan contra el íntegro;

le tiran sin temor y sin aviso.

5Unos a otros se animan en sus planes malvados,

calculan cómo tender sus trampas;

y hasta dicen: «¿Quién las verá?».

6Maquinan injusticias y dicen:

«¡Hemos tramado un plan perfecto!».

¡Cuán incomprensibles son

la mente y el corazón humano!

7Pero Dios les disparará sus flechas

y sin aviso caerán heridos.

8Su propia lengua será su ruina

y quien los vea se burlará de ellos.

9La humanidad entera sentirá temor:

proclamará las proezas de Dios

y meditará en sus obras.

10Que se regocijen en el Señor los justos;

que busquen refugio en él;

¡que lo alaben todos los de corazón sincero!