Salimo 64
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
1Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga;
tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
2Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa,
ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.
3Iwo amanola malilime awo ngati malupanga,
amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
4Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa;
amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.
5Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa,
amayankhula zobisa misampha yawo;
ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
6Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati,
“Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!”
Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.
7Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi;
mwadzidzidzi adzakanthidwa.
8Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa
ndi kuwasandutsa bwinja;
onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.
9Anthu onse adzachita mantha;
adzalengeza ntchito za Mulungu
ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
10Lolani wolungama akondwere mwa Yehova
ndi kubisala mwa Iye,
owongoka mtima onse atamande Iye!
Псалам 64
Хоровођи. Псалам Давидов.
1Чуј, о, Боже, глас мој, жалопојку моју;
од страхоте противника живот ми сачувај.
2Заклони ме од сплетки злотвора,
од халабуке починитеља злобе.
3Језике своје попут мача они оштре,
одапињу стреле своје – речи заједљиве –
4да из скривених места
гађају човека без мане;
и наједном гађају га
и страха немају.
5Соколе се међу собом на зле ствари,
договарају се да прикрију клопке,
па говоре: „Ко ће да их види?“
6Сплићу неправду:
„Смислили смо! Сплетка је сплетена.“
Дубоки су човекова нутрина и срце.
7Али Бог ће их стрелом гађати
и наједном рањени ће бити.
8О свој језик саплеће се,
задрхтаће свако ко их гледа;
9препашће се сав род људски,
објавиће дело Божије
и његово дело разматраће.
10Радоваће се праведник у Господу,
у њему ће уточиште наћи,
па ће се хвалити свако срца честитога.