Masalimo 63 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 63:1-11

Salimo 63

Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda.

1Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga,

moona mtima ine ndimakufunafunani;

moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu,

thupi langa likulakalaka inu,

mʼdziko lowuma ndi lotopetsa

kumene kulibe madzi.

2Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika

ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.

3Chifukwa chikondi chanu

ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.

4Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga,

ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.

5Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona.

Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.

6Pa bedi panga ndimakumbukira inu;

ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.

7Chifukwa ndinu thandizo langa,

ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.

8Moyo wanga umakangamira Inu;

dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.

9Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa;

adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.

10Iwo adzaperekedwa ku lupanga

ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.

11Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu;

onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo,

koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.

New International Version

Psalms 63:1-11

Psalm 63In Hebrew texts 63:1-11 is numbered 63:2-12.

A psalm of David. When he was in the Desert of Judah.

1You, God, are my God,

earnestly I seek you;

I thirst for you,

my whole being longs for you,

in a dry and parched land

where there is no water.

2I have seen you in the sanctuary

and beheld your power and your glory.

3Because your love is better than life,

my lips will glorify you.

4I will praise you as long as I live,

and in your name I will lift up my hands.

5I will be fully satisfied as with the richest of foods;

with singing lips my mouth will praise you.

6On my bed I remember you;

I think of you through the watches of the night.

7Because you are my help,

I sing in the shadow of your wings.

8I cling to you;

your right hand upholds me.

9Those who want to kill me will be destroyed;

they will go down to the depths of the earth.

10They will be given over to the sword

and become food for jackals.

11But the king will rejoice in God;

all who swear by God will glory in him,

while the mouths of liars will be silenced.