Masalimo 63 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 63:1-11

Salimo 63

Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda.

1Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga,

moona mtima ine ndimakufunafunani;

moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu,

thupi langa likulakalaka inu,

mʼdziko lowuma ndi lotopetsa

kumene kulibe madzi.

2Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika

ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.

3Chifukwa chikondi chanu

ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.

4Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga,

ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.

5Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona.

Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.

6Pa bedi panga ndimakumbukira inu;

ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.

7Chifukwa ndinu thandizo langa,

ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.

8Moyo wanga umakangamira Inu;

dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.

9Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa;

adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.

10Iwo adzaperekedwa ku lupanga

ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.

11Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu;

onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo,

koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 63:1-11

第 63 篇

渴慕上帝

大卫在旷野时作的诗。

1上帝啊,你是我的上帝,

我迫切地寻求你!

在干旱荒凉之地,

我的心渴慕你,渴慕你!

2我曾在你的圣所瞻仰你的荣面,

目睹你的权能和荣耀。

3你的慈爱比生命更宝贵,

我的嘴唇要赞美你。

4我一生都要赞美你,

奉你的名举手祷告。

5我心满意足,如享盛宴,

唱起欢快的歌赞美你。

6我躺在床上的时候思念你,

整夜地思想你。

7因为你是我的帮助,

我在你翅膀的荫庇下欢歌。

8我的心依恋你,

你的右手扶持我。

9那些图谋毁灭我的人必下到阴间。

10他们必丧身刀下,

成为豺狼的食物。

11但王要因上帝而欢欣,

凡信靠祂的人必欢喜快乐,

说谎者的口必被封住。