Masalimo 63 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 63:1-11

Salimo 63

Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda.

1Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga,

moona mtima ine ndimakufunafunani;

moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu,

thupi langa likulakalaka inu,

mʼdziko lowuma ndi lotopetsa

kumene kulibe madzi.

2Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika

ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.

3Chifukwa chikondi chanu

ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.

4Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga,

ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.

5Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona.

Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.

6Pa bedi panga ndimakumbukira inu;

ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.

7Chifukwa ndinu thandizo langa,

ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.

8Moyo wanga umakangamira Inu;

dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.

9Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa;

adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.

10Iwo adzaperekedwa ku lupanga

ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.

11Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu;

onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo,

koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 63:1-12

Længsel efter Herren

1En sang af David, da han opholdt sig i Judæas ødemark.

2Gud, du er min Gud, og jeg opsøger dig.

Min sjæl tørster efter fællesskab med dig.

Hele min krop sukker efter et møde med dig

i dette afsvedne og tørre land.

3Jeg har oplevet din nærhed i helligdommen,

jeg har set din magt og herlighed.

4At opleve din godhed er mere værd end livet.

Derfor vil jeg altid lovsynge dig.

5Jeg vil takke dig, så længe jeg lever,

løfte mine hænder i tilbedelse til dig.

6Du mætter min sjæl med udsøgte retter,

jeg lovsynger dig med fryd i hjertet.

7Når jeg ligger i min seng, mindes jeg din storhed,

jeg tænker på din nåde, når jeg vågner om natten.

8Jeg husker, hvor ofte du har hjulpet mig,

jeg fryder mig under dine vingers skygge.

9Jeg klynger mig til dig,

og du holder mig i dine stærke arme.

10Mine fjender prøver at dræbe mig,

men de skal styrtes i dødsriget.

11De skal falde for sværdet

og blive føde for sjakaler.

12Men jeg vil glæde mig over min Gud.

Enhver, der stoler på ham, har grund til at juble,

men de falske bedragere må forblive tavse.