Masalimo 62 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 62:1-12

Salimo 62

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide.

1Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha;

chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.

2Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;

Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.

3Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti?

Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba,

ngati mpanda wogwedezeka?

4Iwo akufunitsitsa kumugwetsa

kuti achoke pa malo ake apamwamba.

Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza.

Ndi pakamwa pawo amadalitsa

koma mʼmitima yawo amatemberera.

5Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga;

chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.

6Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;

Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.

7Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu:

Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.

8Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu;

khuthulani mitima yanu kwa Iye,

pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu.

Sela

9Anthu wamba ndi mpweya chabe;

anthu apamwamba ndi bodza chabe;

ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe;

iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe

10Musadalire kulanda mwachinyengo

kapena katundu wobedwa;

ngakhale chuma chanu chichuluke,

musayike mtima wanu pa icho.

11Mulungu wayankhula kamodzi,

ine ndamvapo zinthu ziwiri;

choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,

12komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika.

Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu

molingana ndi ntchito zake.

New International Version – UK

Psalms 62:1-12

Psalm 62In Hebrew texts 62:1-12 is numbered 62:2-13.

For the director of music. For Jeduthun. A psalm of David.

1Truly my soul finds rest in God;

my salvation comes from him.

2Truly he is my rock and my salvation;

he is my fortress, I shall never be shaken.

3How long will you assault me?

Would all of you throw me down –

this leaning wall, this tottering fence?

4Surely they intend to topple me

from my lofty place;

they take delight in lies.

With their mouths they bless,

but in their hearts they curse.62:4 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verse 8.

5Yes, my soul, find rest in God;

my hope comes from him.

6Truly he is my rock and my salvation;

he is my fortress, I shall not be shaken.

7My salvation and my honour depend on God62:7 Or / God Most High is my salvation and my honour;

he is my mighty rock, my refuge.

8Trust in him at all times, you people;

pour out your hearts to him,

for God is our refuge.

9Surely the lowborn are but a breath,

the highborn are but a lie.

If weighed on a balance, they are nothing;

together they are only a breath.

10Do not trust in extortion

or put vain hope in stolen goods;

though your riches increase,

do not set your heart on them.

11One thing God has spoken,

two things I have heard:

‘Power belongs to you, God,

12and with you, Lord, is unfailing love’;

and, ‘You reward everyone

according to what they have done.’