Masalimo 62 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 62:1-12

Salimo 62

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide.

1Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha;

chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.

2Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;

Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.

3Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti?

Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba,

ngati mpanda wogwedezeka?

4Iwo akufunitsitsa kumugwetsa

kuti achoke pa malo ake apamwamba.

Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza.

Ndi pakamwa pawo amadalitsa

koma mʼmitima yawo amatemberera.

5Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga;

chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.

6Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;

Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.

7Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu:

Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.

8Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu;

khuthulani mitima yanu kwa Iye,

pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu.

Sela

9Anthu wamba ndi mpweya chabe;

anthu apamwamba ndi bodza chabe;

ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe;

iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe

10Musadalire kulanda mwachinyengo

kapena katundu wobedwa;

ngakhale chuma chanu chichuluke,

musayike mtima wanu pa icho.

11Mulungu wayankhula kamodzi,

ine ndamvapo zinthu ziwiri;

choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,

12komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika.

Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu

molingana ndi ntchito zake.

New International Reader’s Version

Psalm 62:1-12

Psalm 62

For the director of music. For Jeduthun. A psalm of David.

1It is surely true that I find my rest in God.

He is the God who saves me.

2It is surely true that he is my rock. He is the God who saves me.

He is like a fort to me. I will always be secure.

3How long will you enemies attack me?

Will all of you throw me down?

I’m like a leaning wall.

I’m like a fence about to fall.

4Surely my enemies only want to pull me down

from my place of honor.

They take delight in telling lies.

They bless me with what they say.

But in their hearts they ask for bad things to happen to me.

5Yes, I must find my rest in God.

He is the God who gives me hope.

6It is surely true that he is my rock and the God who saves me.

He is like a fort to me, so I will always be secure.

7I depend on God to save me and to honor me.

He is my mighty rock and my place of safety.

8Trust in him at all times, you people.

Tell him all your troubles.

God is our place of safety.

9Surely ordinary people are only a breath.

Important people are not what they seem to be.

If they were weighed on a scale, they wouldn’t amount to anything.

Together they are only a breath.

10Don’t trust in money you have taken from others.

Don’t put false hope in things you have stolen.

Even if your riches grow,

don’t put your trust in them.

11God, I have heard you say two things.

One is that power belongs to you, God.

12The other is that your love, Lord, never ends.

You will reward everyone

in keeping with what they have done.