Masalimo 62 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 62:1-12

Salimo 62

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide.

1Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha;

chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.

2Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;

Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.

3Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti?

Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba,

ngati mpanda wogwedezeka?

4Iwo akufunitsitsa kumugwetsa

kuti achoke pa malo ake apamwamba.

Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza.

Ndi pakamwa pawo amadalitsa

koma mʼmitima yawo amatemberera.

5Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga;

chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.

6Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;

Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.

7Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu:

Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.

8Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu;

khuthulani mitima yanu kwa Iye,

pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu.

Sela

9Anthu wamba ndi mpweya chabe;

anthu apamwamba ndi bodza chabe;

ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe;

iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe

10Musadalire kulanda mwachinyengo

kapena katundu wobedwa;

ngakhale chuma chanu chichuluke,

musayike mtima wanu pa icho.

11Mulungu wayankhula kamodzi,

ine ndamvapo zinthu ziwiri;

choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,

12komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika.

Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu

molingana ndi ntchito zake.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 62:1-13

Tillid til Guds beskyttelse

1Til korlederen Jedutun. En sang af David.

2Jeg sætter al min lid til Gud,

for kun han kan frelse mig.

3Ja, han er mit skjold og mit værn,

hos ham kan jeg være tryg.

4Hvor længe vil I angribe en sagesløs mand

og forsøge at slå mig omkuld?

I ser på mig som en hældende mur

eller et faldefærdigt stakit.

5I ønsker at styrte mig fra min høje position,

og I er fulde af løgn og bedrag.

Jeres ord virker venlige,

men indvendig er I fulde af foragt.

6Jeg sætter al min lid til Gud,

for kun han giver mig håb.

7Ja, han er mit skjold og mit værn,

hos ham kan jeg være tryg.

8Det er Gud, der hjælper mig og giver mig ære.

Han er mit værn og mit tilflugtssted.

9Stol altid på Gud, mit folk.

Udøs jeres hjerte for ham,

for han er et værn for os alle.

10Menneskers tanker er tomhed,

deres hæderlighed er blot et bedrag.

Hvis man forsøgte at måle deres troskab,

ville det ikke give udslag på vægten.

11Man kan blive rig på uretmæssig vis,

men det giver ikke tryghed og fred.

Selv om din velstand skulle vokse,

må du ikke bygge dit liv på den.

12-13Gud har fortalt os to grundlæggende ting

om sit eget guddommelige væsen:

Han er mægtig, trofast og kærlig,

og han dømmer alle efter deres handlinger.