Masalimo 61 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 61:1-8

Salimo 61

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe.

1Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu;

mvetserani pemphero langa.

2Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu

ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka;

tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.

3Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga,

nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.

4Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya

ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.

5Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga;

mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.

6Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu,

zaka zake kwa mibado yochuluka.

7Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya;

ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.

8Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu

ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.

New International Version – UK

Psalms 61:1-8

Psalm 61In Hebrew texts 61:1-8 is numbered 61:2-9.

For the director of music. With stringed instruments. Of David.

1Hear my cry, O God;

listen to my prayer.

2From the ends of the earth I call to you,

I call as my heart grows faint;

lead me to the rock that is higher than I.

3For you have been my refuge,

a strong tower against the foe.

4I long to dwell in your tent for ever

and take refuge in the shelter of your wings.61:4 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here.

5For you, God, have heard my vows;

you have given me the heritage of those who fear your name.

6Increase the days of the king’s life,

his years for many generations.

7May he be enthroned in God’s presence for ever;

appoint your love and faithfulness to protect him.

8Then I will ever sing in praise of your name

and fulfil my vows day after day.