Masalimo 61 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 61:1-8

Salimo 61

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe.

1Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu;

mvetserani pemphero langa.

2Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu

ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka;

tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.

3Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga,

nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.

4Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya

ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.

5Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga;

mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.

6Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu,

zaka zake kwa mibado yochuluka.

7Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya;

ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.

8Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu

ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.

La Bible du Semeur

Psaumes 61:1-9

Abrite-moi sous ton aile !

1Au chef de chœur. Un psaume de David à chanter avec accompagnement d’instruments à cordes.

2Entends mon cri, ô Dieu !

Ecoute ma prière !

3Des confins de la terre, ╵je fais appel à toi, ╵car je suis abattu.

Conduis-moi au rocher ╵que je ne puis atteindre !

4Car tu es pour moi un refuge,

une tour forte ╵face à mes ennemis !

5Je voudrais demeurer ╵pour toujours dans ta tente61.5 Dans le tabernacle, c’est-à-dire là où Dieu manifeste sa présence (voir 15.1 ; 27.4 ; 2 S 6.17 ; 7.2 ; 1 R 1.39 ; 2.28-30).,

me réfugier, ╵bien caché, sous tes ailes.

Pause

6Oui, ô Dieu, mes souhaits, ╵tu les as exaucés,

et tu m’as accordé la part ╵que tu réserves à ceux qui te craignent61.6 Autre traduction : et tu as accordé à ceux qui te craignent la part que tu leur réserves..

7Ajoute de longs jours ╵aux jours de notre roi,

et que ses années couvrent ╵plusieurs générations !

8Qu’il siège pour toujours ╵sous le regard de Dieu !

Ordonne à ton amour, ╵à ta fidélité, ╵de prendre soin de lui !

9Alors je chanterai ╵sans cesse en ton honneur,

j’accomplirai mes vœux ╵jour après jour.