Masalimo 60 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 60:1-12

Salimo 60

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere.

1Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza.

Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!

2Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba,

konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.

3Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto;

inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.

4Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera

kuti tisonkhanireko pothawa uta.

5Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja,

kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.

6Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika:

“Mwakupambana ndidzagawa Sekemu

ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.

7Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso;

Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera,

Yuda ndi ndodo yanga yaufumu

8Mowabu ndi mbale yanga yosambira,

pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga,

pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”

9Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa?

Ndani adzanditsogolera ku Edomu?

10Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife

ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.

11Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu,

pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.

12Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano

ndipo tidzapondaponda adani athu.

O Livro

Salmos 60:1-12

Salmo 60

(Sl 108.6-13)

Salmo de David. Segundo a melodia “Os lírios”. Poema de instrução. Quando David lutou contra os arameus da Mesopotâmia e os arameus de Zobá, e Joabe, ao regressar, matou no vale do Sal doze mil edomitas.

1Deus, tu rejeitaste-nos e dispersaste-nos;

tens estado zangado connosco,

mas volta-te de novo para nós.

2Fizeste tremer esta terra, dividiste-a em pedaços;

cura-a, pois está abalada até nos fundamentos.

3Fizeste-nos passar por coisas muito duras;

deste-nos a beber um vinho que enlouquece.

4Deste uma bandeira a todos os que te temem,

para que a levantem bem alto pela causa da verdade. (Pausa)

5Salva-nos, para que o povo que amas seja livre!

Ouve-nos e livra-nos pela força do teu braço!

6Deus jurou pela sua santidade:

“É justo que me encha de alegria;

hei de repartir Siquem e medir o vale de Sucote.

7Gileade e Manassés ainda são meus;

Efraim é o apoio da minha força

e Judá me dará governantes.

8Moabe é para mim uma bacia de lavar

e Edom como o sítio onde me descalço.

Sobre a Filisteia bradarei vitória.”

9Quem me conduzirá à cidade fortificada?

Quem me guiará até Edom?

10Deus o fará, ainda que nos tenha rejeitado

e nos tenha abandonado aos exércitos do inimigo.

11Auxilia-nos em tempos de aperto,

pois de nada vale o socorro humano!

12Com Deus faremos coisas formidáveis;

ele esmagará os nossos inimigos.