Masalimo 60 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 60:1-12

Salimo 60

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere.

1Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza.

Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!

2Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba,

konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.

3Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto;

inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.

4Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera

kuti tisonkhanireko pothawa uta.

5Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja,

kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.

6Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika:

“Mwakupambana ndidzagawa Sekemu

ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.

7Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso;

Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera,

Yuda ndi ndodo yanga yaufumu

8Mowabu ndi mbale yanga yosambira,

pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga,

pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”

9Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa?

Ndani adzanditsogolera ku Edomu?

10Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife

ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.

11Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu,

pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.

12Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano

ndipo tidzapondaponda adani athu.

New International Version – UK

Psalms 60:1-12

Psalm 60In Hebrew texts 60:1-12 is numbered 60:3-14.

For the director of music. To the tune of ‘The Lily of the Covenant’. A miktamTitle: Probably a literary or musical term of David. For teaching. When he fought Aram NaharaimTitle: That is, Arameans of North-west Mesopotamia and Aram Zobah,Title: That is, Arameans of central Syria and when Joab returned and struck down twelve thousand Edomites in the Valley of Salt.

1You have rejected us, God, and burst upon us;

you have been angry – now restore us!

2You have shaken the land and torn it open;

mend its fractures, for it is quaking.

3You have shown your people desperate times;

you have given us wine that makes us stagger.

4But for those who fear you, you have raised a banner

to be unfurled against the bow.60:4 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here.

5Save us and help us with your right hand,

that those you love may be delivered.

6God has spoken from his sanctuary:

‘In triumph I will parcel out Shechem

and measure off the Valley of Sukkoth.

7Gilead is mine, and Manasseh is mine;

Ephraim is my helmet,

Judah is my sceptre.

8Moab is my washbasin,

on Edom I toss my sandal;

over Philistia I shout in triumph.’

9Who will bring me to the fortified city?

Who will lead me to Edom?

10Is it not you, God, you who have now rejected us

and no longer go out with our armies?

11Give us aid against the enemy,

for human help is worthless.

12With God we shall gain the victory,

and he will trample down our enemies.