Masalimo 60 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 60:1-12

Salimo 60

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere.

1Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza.

Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!

2Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba,

konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.

3Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto;

inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.

4Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera

kuti tisonkhanireko pothawa uta.

5Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja,

kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.

6Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika:

“Mwakupambana ndidzagawa Sekemu

ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.

7Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso;

Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera,

Yuda ndi ndodo yanga yaufumu

8Mowabu ndi mbale yanga yosambira,

pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga,

pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”

9Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa?

Ndani adzanditsogolera ku Edomu?

10Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife

ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.

11Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu,

pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.

12Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano

ndipo tidzapondaponda adani athu.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Забур 60:1-9

Песнь 60

1Дирижёру хора. На струнных инструментах. Песнь Довуда.

2Всевышний, услышь мой крик,

внемли молитве моей!

3С края земли я к Тебе взываю;

сердце моё в унынии.

Возведи меня на скалу, которая мне недоступна,

4ведь Ты – прибежище моё,

крепкая башня от врага.

5Да живу я вечно в храме Твоём

и под кровом крыльев Твоих покоюсь. Пауза

6Всевышний, Ты услышал мои обеты;

Ты дал мне наследие тех, кто боится Твоего имени.

7Умножь дни жизни царя,

продли его годы из поколения в поколение.

8Да восседает он вечно перед Всевышним;

сохрани его Своей милостью и истиной.

9И буду я Твоё имя воспевать всегда,

день за днём исполняя мои обеты.