Masalimo 6 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 6:1-10

Salimo 6

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide.

1Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu,

kapena kundilanga mu ukali wanu.

2Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka;

Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.

3Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu.

Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?

4Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse;

pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

5Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira;

Amakutamandani ndani ali ku manda?

6Ine ndatopa ndi kubuwula;

usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga;

ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.

7Maso anga atupa chifukwa cha chisoni;

akulephera kuona chifukwa cha adani anga.

8Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa,

pakuti Yehova wamva kulira kwanga.

9Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo;

Yehova walandira pemphero langa.

10Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha;

adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.

New International Reader’s Version

Psalm 6:1-10

Psalm 6

For the director of music. According to sheminith. A psalm of David to be played on stringed instruments.

1Lord, don’t correct me when you are angry.

Don’t punish me when you are very angry.

2Lord, have mercy on me. I’m so weak.

Lord, heal me. My body is full of pain.

3My soul is very troubled.

Lord, how long will it be until you save me?

4Lord, turn to me and help me.

Save me. Your love never fails.

5Dead people can’t call out your name.

How can they praise you when they are in the grave?

6My groaning has worn me out.

All night long my tears flood my bed.

My bed is wet because of my crying.

7I’m so sad I can’t see very well.

My eyesight gets worse because of all my enemies.

8Get away from me, all you who do evil.

The Lord has heard my weeping.

9The Lord has heard my cry for his mercy.

The Lord accepts my prayer.

10All my enemies will be covered with shame and trouble.

They will turn back in shame. It will happen suddenly.