Masalimo 58 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 58:1-11

Salimo 58

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide.

1Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama?

Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?

2Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama,

ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.

3Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera;

kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.

4Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka,

ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.

5Imene simva liwu la munthu wamatsenga,

ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.

6Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu,

Yehova khadzulani mano a mikango!

7Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda

pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.

8Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda;

ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.

9Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku,

kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.

10Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango,

pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.

11Ndipo anthu adzanena kuti,

“Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho;

zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”

New International Reader’s Version

Psalm 58:1-11

Psalm 58

For the director of music. A miktam of David to the tune of “Do Not Destroy.”

1Are you rulers really fair when you speak?

Do you judge people honestly?

2No, in your hearts you plan to be unfair.

With your hands you do terrible things on the earth.

3Even from birth those who are evil go down the wrong path.

From the day they are born they go the wrong way and spread lies.

4Their words are like the poison of a snake.

They are like the poison of a cobra that has covered up its ears.

5It won’t listen to a snake charmer’s tune,

even if the charmer plays very well.

6God, break the teeth in the mouths of those sinners!

Lord, tear out the sharp teeth of those lions!

7Let those people disappear like water that flows away.

When they draw their bows, let their arrows fall short of the target.

8Let them be like a slug that melts away as it moves along.

Let them be like a baby that is born dead and never sees the sun.

9Evil people will be swept away before burning thorns can heat a pot.

And it doesn’t matter if the thorns are green or dry.

10Godly people will be glad when those who have hurt them are paid back.

They will dip their feet in the blood of those who do evil.

11Then people will say,

“The godly will get their reward.

There really is a God who judges the earth.”