Masalimo 58 – CCL & NAV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 58:1-11

Salimo 58

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide.

1Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama?

Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?

2Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama,

ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.

3Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera;

kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.

4Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka,

ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.

5Imene simva liwu la munthu wamatsenga,

ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.

6Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu,

Yehova khadzulani mano a mikango!

7Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda

pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.

8Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda;

ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.

9Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku,

kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.

10Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango,

pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.

11Ndipo anthu adzanena kuti,

“Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho;

zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”

Ketab El Hayat

مزمور 58:1-11

الْمَزْمُورُ الثَّامِنُ وَالْخَمْسُونَ

لِقَائِدِ الْمُنْشِدِينَ – عَلَى لَا تُهْلِكْ. مُذَهَّبَةٌ لِدَاوُدَ

1أَحَقّاً تَنْطِقُونَ بِالْحَقِّ أَيُّهَا الْحُكَّامُ، وَتَقْضُونَ بِالاسْتِقَامَةِ يَا بَنِي الْبَشَرِ؟ 2لا! إِنَّمَا تُضْمِرُونَ الْبَاطِلَ فِي الْقَلْبِ وَتَرْتَكِبُ أَيْدِيكُمُ الظُّلْمَ فِي الأَرْضِ. 3زَاغَ الأَشْرَارُ وَهُمْ مَا بَرِحُوا فِي بُطُونِ أُمَّهَاتِهِمْ، وَضَلُّوا نَاطِقِينَ بِالْكَذِبِ مُنْذُ أَنْ وُلِدُوا. 4فِيهِمْ سُمٌّ كَسُمِّ الْحَيَّاتِ، يَسُدُّونَ آذَانَهُمْ كَالأَفَاعِي الصَّمَّاءِ، 5الَّتِي لَا تَسْمَعُ لِصَوْتِ الْحُوَاةِ، وَلَا لِصَوْتِ السَّاحِرِ الْمَاهِرِ. 6هَشِّمْ أَسْنَانَهُمْ فِي أَفْوَاهِهِمْ يَا اللهُ. حَطِّمْ أَنْيَابَ الأَشْبَالِ. 7لِيَتَلاشَوْا كَالْمَاءِ الْمُرَاقِ، وَلْتَتَكَسَّرْ رُؤُوسُ سِهَامِهِمْ عِنْدَمَا يُصَوِّبُونَهَا. 8لِيَتَلاشَوْا مِثْلَ الْقَوَاقِعِ فِي أَثْنَاءِ زَحْفِهَا، وَكَالْجَنِينِ الْمُجْهَضِ لَا يُعَايِنُونَ الشَّمْسَ. 9وَقَبْلَ أَنْ تُحِسَّ قُدُورُكُمْ بِنَارِ الأَشْوَاكِ تَحْتَهَا، يَكْتَسِحُ اللهُ كَبِيرَهُمْ وَصَغِيرَهُمْ بِعَاصِفَةِ غَضَبِهِ، 10يَفْرَحُ الأَبْرَارُ حِينَ يَرَوْنَ عِقَابَ الأَشْرَارِ، وَيَغْسِلُونَ أَقْدَامَهُمْ بِدَمِهِمْ. 11فَيَقُولُ النَّاسُ: «حَقّاً إِنَّ للِصِّدِّيقِ مُكَافَأَةً، وَإِنَّ فِي الأَرْضِ إِلَهاً يَقْضِي».