Masalimo 58 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 58:1-11

Salimo 58

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide.

1Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama?

Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?

2Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama,

ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.

3Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera;

kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.

4Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka,

ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.

5Imene simva liwu la munthu wamatsenga,

ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.

6Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu,

Yehova khadzulani mano a mikango!

7Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda

pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.

8Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda;

ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.

9Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku,

kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.

10Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango,

pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.

11Ndipo anthu adzanena kuti,

“Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho;

zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 58:1-12

Dom over onde magthavere

1Til korlederen: En sang af David.

2Mon I fyrster ved, hvad der er ret og rigtigt?

Mon I behandler folk retfærdigt?

3Nej, I har kun ondskab i tanke,

I giver volden frit løb i landet.

4I har været onde fra fødslen af,

fra barnsben har I været fulde af løgn.

5I udspyr slangegift og vil ikke lytte til Gud.

I ligner en døv kobra,

6der ikke kan høre slangetæmmeren,

lige meget hvor højt han spiller.

7Knus kæberne på de grusomme løver, Herre.

Bræk alle deres skarpe tænder, Gud.

8Lad dem forsvinde som vand i ørkenen,

lad dem visne som græs i tørtiden.

9Lad dem blive til slim som sneglen,

lad dem ende som dødfødte fostre,

der aldrig får lyset at se.

10Gud vil feje de onde af vejen,

hurtigere end brændet kan få gryden i kog.58,10 Teksten er uklar.

11De gudfrygtige glæder sig, når retten sejrer.

De får lov at vade i de gudløses blod.

12Da skal folk udbryde:

„Ja, de gudfrygtige bliver belønnet til sidst.

Der er en Gud, som sørger for retfærdighed på jorden.”