Masalimo 57 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 57:1-11

Salimo 57

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga.

1Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo,

pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo.

Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu

mpaka chiwonongeko chitapita.

2Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba,

kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.

3Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa,

kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri.

Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.

4Ine ndili pakati pa mikango,

ndagona pakati pa zirombo zolusa;

anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi,

malilime awo ndi malupanga akuthwa.

5Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba;

mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.

6Iwo anatchera mapazi anga ukonde

ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa.

Anakumba dzenje mʼnjira yanga

koma agweramo okha mʼmenemo.

7Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu

mtima wanga ndi wokhazikika.

Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.

8Dzuka moyo wanga!

Dzukani zeze ndi pangwe!

Ndidzadzuka mʼbandakucha.

9Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu,

ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.

10Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba;

kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.

11Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba,

mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.

New Russian Translation

Псалтирь 57:1-12

Псалом 57

1Дирижеру хора. На мотив «Не погуби». Мольба Давида.

2Подлинно ли вы, правители,

говорите беспристрастно?

Справедливо ли судите меж людьми?

3Нет, неправду вы замышляете,

ваши руки творят на земле произвол.

4От утробы матери нечестивые – среди отступников;

с рождения сбились с пути и обманывают.

5Яд их подобен яду змеиному,

яду глухой кобры, что уши свои затыкает

6и не слышит голоса заклинателя,

как бы тот ни был искусен.

7Раздроби зубы у них во рту, о Боже;

вырви, Господи, клыки у львов!

8Да исчезнут, как высохшая вода;

пусть будут как надломленные стрелы в натянутом луке57:8 Смысл этого места в еврейском тексте неясен.,

9как улитка, что растает, слизью изойдя,

как мертворожденный, что не увидит света.

10Прежде чем ваши котлы согреет горящий терн –

зелен он или сух – нечестивые будут погублены57:10 Смысл этого стиха в еврейском тексте неясен..

11Праведники возрадуются, когда увидят возмездие,

когда омоют стопы в крови нечестивых.

12И будут тогда говорить:

«Поистине, праведным есть награда;

поистине, есть Бог, судящий на земле».