Masalimo 56 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 56:1-13

Salimo 56

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati.

1Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri;

tsiku lonse akundithira nkhondo.

2Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse,

ambiri akumenyana nane monyada.

3Ndikachita mantha

ndimadalira Inu.

4Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda,

mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha.

Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?

5Tsiku lonse amatembenuza mawu anga;

nthawi zonse amakonza zondivulaza.

6Iwo amakambirana, amandibisalira,

amayangʼanitsitsa mayendedwe anga

ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.

7Musalole konse kuti athawe;

mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.

8Mulembe za kulira kwanga,

mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu.

Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?

9Adani anga adzabwerera mʼmbuyo

pamene ndidzalirira kwa Inu.

Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.

10Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda,

mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,

11mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha.

Kodi munthu angandichite chiyani?

12Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu;

ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.

13Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa

ndi mapazi anga kuti ndingagwe,

kuti ndiyende pamaso pa Mulungu

mʼkuwala kwa moyo.

Luganda Contemporary Bible

Zabbuli 56:1-13

Zabbuli 56

Ya Mukulu wa Bayimbi. Zabbuli ya Dawudi. Abafirisuuti bwe baamukwatira mu Gaasi.

156:1 Zab 57:1-3Onsaasire, Ayi Katonda, kubanga abalabe bange banjigganya;

buli lunaku bannumba n’amaanyi.

256:2 a Zab 57:3 b Zab 35:1Abalabe bange bannondoola,

bangi bannwanyisa nga bajjudde amalala.

356:3 Zab 55:4-5Buli lwe ntya,

neesiga ggwe.

456:4 Zab 118:6; Beb 13:6Nditendereza Katonda ne nyweerera mu kigambo kye,

ye Katonda gwe neesiga; siityenga.

Abantu obuntu bagenda kunkolako ki?

556:5 Zab 41:7Olunaku lwonna bye njogera babifuulafuula;

ebbanga lyonna baba basala nkwe kunkola kabi.

656:6 a Zab 59:3 b Zab 71:10Beekobaana ne bateesa,

banneekwekerera ne bawuliriza enswagiro zange;

nga bannindirira banzite.

756:7 Zab 36:12; 55:23Tobakkiriza kudduka ne bawona;

mu busungu bwo, Ayi Katonda, osuule amawanga.

856:8 Mal 3:16Emirundi gye ntawaanyizibwa nga njaziirana ogimanyi;

amaziga gange gateeke mu ccupa yo!

Wagawandiika.

956:9 a Zab 9:3 b Zab 102:2 c Bar 8:31Bwe nkukoowoola,

abalabe bange nga badduka.

Kino nkimanyi kubanga Katonda ali ku ludda lwange.

10Katonda gwe ntendereza olw’ekisuubizo kye;

Mukama gwe ntendereza olw’ekisuubizo kye;

11Katonda oyo gwe neesiga, siityenga.

Abantu bayinza kunkolako ki?

1256:12 Zab 50:14Ndituukiriza obweyamo bwange gy’oli, Ayi Katonda;

ndikuleetera ebirabo eby’okukwebaza.

1356:13 a Zab 116:8 b Yob 33:30Kubanga emmeeme yange ogiwonyezza okufa.

Ebigere byange tobiwonyezza okwesittala;

ne ndyoka ntambulira mu maaso ga Katonda

mu musana nga ndi mulamu?