Masalimo 56 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 56:1-13

Salimo 56

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati.

1Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri;

tsiku lonse akundithira nkhondo.

2Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse,

ambiri akumenyana nane monyada.

3Ndikachita mantha

ndimadalira Inu.

4Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda,

mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha.

Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?

5Tsiku lonse amatembenuza mawu anga;

nthawi zonse amakonza zondivulaza.

6Iwo amakambirana, amandibisalira,

amayangʼanitsitsa mayendedwe anga

ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.

7Musalole konse kuti athawe;

mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.

8Mulembe za kulira kwanga,

mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu.

Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?

9Adani anga adzabwerera mʼmbuyo

pamene ndidzalirira kwa Inu.

Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.

10Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda,

mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,

11mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha.

Kodi munthu angandichite chiyani?

12Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu;

ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.

13Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa

ndi mapazi anga kuti ndingagwe,

kuti ndiyende pamaso pa Mulungu

mʼkuwala kwa moyo.

Korean Living Bible

시편 56:1-13

하나님을 신뢰하는 기도

(다윗이 가드에서 블레셋 사람들에게 잡혔을 때 지은 시. 성가대 지휘자를 따라 ‘멀리 상수리나무에 앉은 비둘기’ 란 곡조에 맞춰 부른 노래)

1하나님이시여,

나를 불쌍히 여기소서.

사람들이 나를 짓밟고

하루 종일 몰아붙이고 있습니다.

2내 원수들이 종일

나를 추격합니다.

교만하게 나를 대적하는 자

많습니다.

3내가 두려울 때

주를 신뢰하겠습니다.

4내가 하나님을 신뢰하고

주의 말씀을 찬양합니다.

내가 하나님을 신뢰하므로

두려워하지 않겠습니다.

사람에 불과한 자가

나를 어떻게 하겠습니까?

5내 원수들이 하루 종일

내 말을 곡해하며

항상 나를 해할 음모를

꾸미고 있습니다.

6그들이 공모하고 숨어서

내 거동을 일일이 살피며

나를 죽일 기회만 엿보고 있습니다.

7하나님이시여,

그들이 결코 피하지 못하게 하시고

주의 분노로 그들을 벌하소서.

8주는 나의 슬픔을 아십니다.

내 눈물을 주의 병에 담으소서.

내 눈물이

주의 책에 기록되지 않았습니까?

9내가 소리쳐 주를 부를 때

내 원수들이 물러갈 것이므로

내가 이것으로 하나님이

내 편에 계시는 것을 알 것입니다.

10내가 하나님을 신뢰하고

주의 말씀을 찬양합니다.

내가 여호와를 신뢰하고

주의 말씀을 찬양합니다.

11내가 하나님을 신뢰하고

두려워하지 않을 것입니다.

사람이 나를 어찌하겠습니까?

12하나님이시여,

내가 주께 약속한 것이 있으니

감사제를 주께 드리겠습니다.

13주께서는

나를 죽음에서 건져 주시고

넘어지지 않게 하셨으며

나를 56:13 또는 ‘하나님’주 앞에서 생명의 빛 가운데

다니도록 하셨습니다.