Masalimo 56 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 56:1-13

Salimo 56

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati.

1Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri;

tsiku lonse akundithira nkhondo.

2Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse,

ambiri akumenyana nane monyada.

3Ndikachita mantha

ndimadalira Inu.

4Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda,

mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha.

Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?

5Tsiku lonse amatembenuza mawu anga;

nthawi zonse amakonza zondivulaza.

6Iwo amakambirana, amandibisalira,

amayangʼanitsitsa mayendedwe anga

ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.

7Musalole konse kuti athawe;

mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.

8Mulembe za kulira kwanga,

mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu.

Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?

9Adani anga adzabwerera mʼmbuyo

pamene ndidzalirira kwa Inu.

Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.

10Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda,

mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,

11mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha.

Kodi munthu angandichite chiyani?

12Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu;

ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.

13Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa

ndi mapazi anga kuti ndingagwe,

kuti ndiyende pamaso pa Mulungu

mʼkuwala kwa moyo.

Hoffnung für Alle

Psalm 56:1-14

Besiegte Angst

1Ein Lied von David, nach der Melodie: »Die Taube verstummt in der Fremde«. Es stammt aus der Zeit, als die Philister ihn in Gat festgenommen hatten.56,1 Vgl. 1. Samuel 21,11‒16.

2Gott, hab Erbarmen mit mir,

denn man will mich zur Strecke bringen!

Die Feinde bedrängen mich den ganzen Tag.

3Unaufhörlich greifen sie mich an,

viele bekämpfen mich in ihrem Hochmut.

4Doch gerade dann, wenn ich Angst habe,

will ich mich dir anvertrauen.

5Ich lobe Gott für das, was er versprochen hat;

ihm vertraue ich und fürchte mich nicht.

Was kann ein Mensch mir schon antun?

6Unablässig verdrehen sie, was ich sage,

und überlegen, wie sie mir schaden können.

7Überall muss ich mit einem Hinterhalt rechnen. Sie beschatten mich

und warten nur darauf, mich umzubringen.

8Gott, wirf diese Leute56,8 Wörtlich: die Völker. in deinem Zorn zu Boden!

Sollten sie bei so viel Bosheit ungeschoren davonkommen?

9Du siehst doch, wie lange ich schon umherirre!

Jede Träne hast du gezählt,56,9 Wörtlich: Sammle meine Tränen in deinem Schlauch (= Behälter für Flüssigkeiten).

ja, alle sind in deinem Buch festgehalten.

10Sobald ich dich um Hilfe bitte,

werden meine Feinde kleinlaut den Rückzug antreten.

Denn das weiß ich: Du, Gott, bist auf meiner Seite!

11Ich lobe Gott für das, was er versprochen hat,

ja, ich lobe die Zusage des Herrn.

12Ihm vertraue ich und fürchte mich nicht.

Was kann ein Mensch mir schon antun?

13Gott, was ich dir versprochen habe,

will ich jetzt einlösen und dir aus Dank Opfer bringen.

14Denn du hast mich vor dem Tod gerettet,

vor dem Sturz in die Tiefe hast du mich bewahrt.

Ich darf weiterleben – in deiner Nähe.

Du hast mir das Leben neu geschenkt.