Masalimo 56 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 56:1-13

Salimo 56

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati.

1Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri;

tsiku lonse akundithira nkhondo.

2Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse,

ambiri akumenyana nane monyada.

3Ndikachita mantha

ndimadalira Inu.

4Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda,

mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha.

Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?

5Tsiku lonse amatembenuza mawu anga;

nthawi zonse amakonza zondivulaza.

6Iwo amakambirana, amandibisalira,

amayangʼanitsitsa mayendedwe anga

ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.

7Musalole konse kuti athawe;

mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.

8Mulembe za kulira kwanga,

mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu.

Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?

9Adani anga adzabwerera mʼmbuyo

pamene ndidzalirira kwa Inu.

Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.

10Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda,

mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,

11mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha.

Kodi munthu angandichite chiyani?

12Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu;

ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.

13Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa

ndi mapazi anga kuti ndingagwe,

kuti ndiyende pamaso pa Mulungu

mʼkuwala kwa moyo.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 56:1-13

第 56 篇

信靠上帝的祷告

大卫作的诗,交给乐长,调用“远方无声鸽”,大卫在迦特被非利士人抓住时所作。

1上帝啊,求你怜悯我,

因为仇敌攻击我,整日迫害我。

2我的仇敌整日攻击我,

许多人狂妄地迫害我。

3我害怕的时候,

仍要倚靠你。

4我赞美上帝的应许,

我信靠祂,就不惧怕,

区区世人能把我怎样?

5他们整天歪曲我的话,

总是图谋害我。

6他们勾结起来,

暗中监视我的行踪,

伺机害我。

7上帝啊,

不要让这些作恶的人逃脱,

求你在怒中毁灭他们。

8你知道我的哀伤,

你把我的眼泪收在袋中。

我的遭遇都记录在你的册子上。

9我向你求救的时候,

敌人都落荒而逃。

我知道上帝是我的帮助。

10我因上帝的应许而赞美祂,

我因耶和华的应许而赞美祂。

11我信靠上帝,就不惧怕,

区区世人能把我怎样?

12上帝啊,

我要恪守向你发的誓言,

献上感恩祭。

13因为你救我脱离死亡,

使我没有跌倒,

让我可以活在你面前,

沐浴生命之光。