Salimo 55
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe.
1Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu,
musakufulatire kupempha kwanga,
2mverani ndipo mundiyankhe.
Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
3chifukwa cha mawu a adani anga,
chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa;
pakuti andidzetsera masautso
ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.
4Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga;
mantha a imfa andigwera.
5Mantha ndi kunjenjemera zandizinga;
mantha aakulu andithetsa nzeru.
6Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda!
Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
7Ndikanathawira kutali
ndi kukakhala mʼchipululu.
8Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo;
kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”
9Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo;
pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
10Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake;
nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
11Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda;
kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.
12Akanakhala mdani akundinyoza, ine
ndikanapirira;
akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane,
ndikanakabisala.
13Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye,
bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
14Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala
pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.
15Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi;
alowe mʼmanda ali amoyo
pakuti choyipa chili pakati pawo.
16Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu,
ndipo Yehova anandipulumutsa.
17Madzulo, mmawa ndi masana
ndimalira mowawidwa mtima,
ndipo Iye amamva mawu anga.
18Iye amandiwombola ine osavulazidwa
pa nkhondo imene yafika kulimbana nane,
ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.
19Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya,
adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga,
chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa
ndipo saopa Mulungu.
20Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake;
iye akuphwanya pangano ake.
21Mawu ake ndi osalala kuposa batala
komabe nkhondo ili mu mtima mwake;
mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta,
komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.
22Tulani nkhawa zanu kwa Yehova
ndipo Iye adzakulimbitsani;
Iye sadzalola kuti wolungama agwe.
23Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa
kulowa mʼdzenje lachiwonongeko;
anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo
sadzakhala moyo theka la masiku awo,
koma ine ndimadalira Inu.
Psalm 55In Hebrew texts 55:1-23 is numbered 55:2-24.
For the director of music. With stringed instruments. A maskilTitle: Probably a literary or musical term of David.
1Listen to my prayer, O God,
do not ignore my plea;
2hear me and answer me.
My thoughts trouble me and I am distraught
3because of what my enemy is saying,
because of the threats of the wicked;
for they bring down suffering on me
and assail me in their anger.
4My heart is in anguish within me;
the terrors of death have fallen on me.
5Fear and trembling have beset me;
horror has overwhelmed me.
6I said, “Oh, that I had the wings of a dove!
I would fly away and be at rest.
7I would flee far away
and stay in the desert;55:7 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and in the middle of verse 19.
8I would hurry to my place of shelter,
far from the tempest and storm.”
9Lord, confuse the wicked, confound their words,
for I see violence and strife in the city.
10Day and night they prowl about on its walls;
malice and abuse are within it.
11Destructive forces are at work in the city;
threats and lies never leave its streets.
12If an enemy were insulting me,
I could endure it;
if a foe were rising against me,
I could hide.
13But it is you, a man like myself,
my companion, my close friend,
14with whom I once enjoyed sweet fellowship
at the house of God,
as we walked about
among the worshipers.
15Let death take my enemies by surprise;
let them go down alive to the realm of the dead,
for evil finds lodging among them.
16As for me, I call to God,
and the Lord saves me.
17Evening, morning and noon
I cry out in distress,
and he hears my voice.
18He rescues me unharmed
from the battle waged against me,
even though many oppose me.
19God, who is enthroned from of old,
who does not change—
he will hear them and humble them,
because they have no fear of God.
20My companion attacks his friends;
he violates his covenant.
21His talk is smooth as butter,
yet war is in his heart;
his words are more soothing than oil,
yet they are drawn swords.
22Cast your cares on the Lord
and he will sustain you;
he will never let
the righteous be shaken.
23But you, God, will bring down the wicked
into the pit of decay;
the bloodthirsty and deceitful
will not live out half their days.
But as for me, I trust in you.