Masalimo 55 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 55:1-23

Salimo 55

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe.

1Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu,

musakufulatire kupempha kwanga,

2mverani ndipo mundiyankhe.

Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru

3chifukwa cha mawu a adani anga,

chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa;

pakuti andidzetsera masautso

ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.

4Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga;

mantha a imfa andigwera.

5Mantha ndi kunjenjemera zandizinga;

mantha aakulu andithetsa nzeru.

6Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda!

Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.

7Ndikanathawira kutali

ndi kukakhala mʼchipululu.

8Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo;

kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”

9Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo;

pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.

10Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake;

nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.

11Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda;

kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.

12Akanakhala mdani akundinyoza, ine

ndikanapirira;

akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane,

ndikanakabisala.

13Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye,

bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.

14Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala

pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.

15Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi;

alowe mʼmanda ali amoyo

pakuti choyipa chili pakati pawo.

16Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu,

ndipo Yehova anandipulumutsa.

17Madzulo, mmawa ndi masana

ndimalira mowawidwa mtima,

ndipo Iye amamva mawu anga.

18Iye amandiwombola ine osavulazidwa

pa nkhondo imene yafika kulimbana nane,

ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.

19Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya,

adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga,

chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa

ndipo saopa Mulungu.

20Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake;

iye akuphwanya pangano ake.

21Mawu ake ndi osalala kuposa batala

komabe nkhondo ili mu mtima mwake;

mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta,

komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.

22Tulani nkhawa zanu kwa Yehova

ndipo Iye adzakulimbitsani;

Iye sadzalola kuti wolungama agwe.

23Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa

kulowa mʼdzenje lachiwonongeko;

anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo

sadzakhala moyo theka la masiku awo,

koma ine ndimadalira Inu.

Luganda Contemporary Bible

Zabbuli 55:1-23

Zabbuli 55

Ya Mukulu wa Bayimbi. Eyimbibwa n’ebivuga eby’enkoba. Zabbuli ya Dawudi.

155:1 Zab 27:9; 61:1Owulirize okusaba kwange, Ayi Katonda,

togaya kwegayirira kwange.

255:2 a Zab 66:19 b Zab 77:3; Is 38:14Ompulire era onziremu,

kubanga ndi mu buzibu, nga nsinda olw’okweraliikirira okunene.

355:3 a 2Sa 16:6-8; Zab 17:9 b Zab 71:11Mpulira amaloboozi g’abalabe bange;

ababi bankanulidde amaaso

ne banvuma nga bajjudde obusungu.

455:4 Zab 116:3Omutima gwange gulumwa nnyo munda yange;

entiisa y’okufa entuukiridde.

555:5 Yob 21:6; Zab 119:120Okutya n’okukankana binnumbye;

entiisa empitiridde.

6Ne njogera nti, Singa nnina ebiwaawaatiro ng’ejjiba,

nandibuuse ne ŋŋenda mpummulako.

7“Nandiraze wala nnyo,

ne mbeera eyo mu ddungu;

855:8 Is 4:6nandiyanguye ne ntuuka mu kifo kyange eky’okuwummuliramu,

eteri kibuyaga na mpewo ekunta n’amaanyi.”

955:9 Yer 6:7Mukama tabulatabula ennimi z’ababi, ozikirize enkwe zaabwe;

kubanga ndaba obukambwe n’okulwanagana mu kibuga.

10Beetooloola bbugwe waakyo emisana n’ekiro,

ne munda mu kyo mujjudde ettima n’ebikolwa ebibi.

1155:11 a Zab 5:9 b Zab 10:7Obutemu n’obussi obwa buli ngeri biri mu kibuga omwo.

Buli lw’oyita mu nguudo zaakyo osanga bulimba bwereere na kutiisibwatiisibwa.

12Singa omulabe wange y’abadde anvuma,

nandikigumiikirizza;

singa oyo atakkiriziganya nange y’annumbaganye n’anduulira,

nandimwekwese.

1355:13 2Sa 15:12; Zab 41:9Naye ggwe munnange,

bwe tuyita, era mukwano gwange ddala!

1455:14 Zab 42:4Gwe twabanga naye mu ssanyu ng’abooluganda,

nga tutambulira mu kibiina ekinene mu nnyumba ya Katonda.

1555:15 a Zab 64:7 b Kbl 16:30, 33Okufa kubatuukirire,

bakke emagombe nga bakyali balamu;

kubanga bajjudde okukola ebibi.

16Naye nze nkoowoola Mukama Katonda,

n’andokola.

1755:17 a Zab 141:2; Bik 3:1 b Zab 5:3Ekiro, ne mu makya ne mu ttuntu,

ndaajana nga bwe nsinda;

n’awulira eddoboozi lyange.

18Amponyezza mu lutalo

nga siriiko kintuseeko

newaakubadde ng’abannwanyisizza babadde bangi.

1955:19 a Ma 33:27 b Zab 78:59Katonda oyo atudde ku ntebe ye ebbanga lyonna,

aliwulira n’ababonereza

abo abatakyusa makubo gaabwe

era abatatya Katonda.

2055:20 a Zab 7:4 b Zab 89:34Agololera emikono gye ku mikwano gye;

n’amenya endagaano ye.

2155:21 a Nge 5:3 b Zab 28:3; 57:4; 59:7By’ayogera bigonvu okusinga omuzigo,

so nga mu mutima gwe alowooza lutalo;

ebigambo bye biweweera okusinga amafuta,

so nga munda mu mutima gwe asowodde bitala byennyini.

2255:22 a Zab 37:5; Mat 6:25-34; 1Pe 5:7 b Zab 37:24Ebizibu byo byonna bireete eri Mukama,

ajja kukuwanirira;

kubanga talireka mutuukirivu kugwa.

2355:23 a Zab 73:18 b Zab 5:6 c Yob 15:32; Nge 10:27 d Zab 25:2Naye ggwe, Ayi Katonda,

olisuula abakola ebibi mu kinnya eky’okuzikirira;

era abatemu n’abalimba bonna

tebagenda kuwangaala kimu kyakubiri eky’obulamu bwabwe.

Naye nze, neesiga ggwe.