Masalimo 55 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 55:1-23

Salimo 55

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe.

1Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu,

musakufulatire kupempha kwanga,

2mverani ndipo mundiyankhe.

Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru

3chifukwa cha mawu a adani anga,

chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa;

pakuti andidzetsera masautso

ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.

4Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga;

mantha a imfa andigwera.

5Mantha ndi kunjenjemera zandizinga;

mantha aakulu andithetsa nzeru.

6Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda!

Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.

7Ndikanathawira kutali

ndi kukakhala mʼchipululu.

8Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo;

kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”

9Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo;

pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.

10Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake;

nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.

11Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda;

kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.

12Akanakhala mdani akundinyoza, ine

ndikanapirira;

akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane,

ndikanakabisala.

13Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye,

bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.

14Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala

pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.

15Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi;

alowe mʼmanda ali amoyo

pakuti choyipa chili pakati pawo.

16Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu,

ndipo Yehova anandipulumutsa.

17Madzulo, mmawa ndi masana

ndimalira mowawidwa mtima,

ndipo Iye amamva mawu anga.

18Iye amandiwombola ine osavulazidwa

pa nkhondo imene yafika kulimbana nane,

ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.

19Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya,

adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga,

chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa

ndipo saopa Mulungu.

20Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake;

iye akuphwanya pangano ake.

21Mawu ake ndi osalala kuposa batala

komabe nkhondo ili mu mtima mwake;

mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta,

komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.

22Tulani nkhawa zanu kwa Yehova

ndipo Iye adzakulimbitsani;

Iye sadzalola kuti wolungama agwe.

23Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa

kulowa mʼdzenje lachiwonongeko;

anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo

sadzakhala moyo theka la masiku awo,

koma ine ndimadalira Inu.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 55:1-23

Salmo 55

Al director musical. Acompáñese con instrumentos de cuerda. Masquil de David.

1Escucha, oh Dios, mi oración;

no pases por alto mi súplica.

2¡Óyeme y respóndeme,

porque mis angustias me perturban!

Me aterran 3las amenazas del enemigo

y la opresión de los impíos,

pues me causan sufrimiento

y en su enojo me insultan.

4Se me estremece el corazón dentro del pecho,

y me invade un pánico mortal.

5Temblando estoy de miedo,

sobrecogido estoy de terror.

6¡Cómo quisiera tener las alas de una paloma

y volar hasta encontrar reposo!

7Me iría muy lejos de aquí;

me quedaría a vivir en el desierto. Selah

8Presuroso volaría a mi refugio,

para librarme del viento borrascoso

y de la tempestad.

9¡Destrúyelos, Señor! ¡Confunde su lengua!

En la ciudad solo veo contiendas y violencia;

10día y noche rondan por sus muros,

y dentro de ella hay intrigas y maldad.

11En su seno hay fuerzas destructivas;

de sus calles no se apartan la opresión y el engaño.

12Si un enemigo me insultara,

yo lo podría soportar;

si un adversario me humillara,

de él me podría yo esconder.

13Pero lo has hecho tú, un hombre como yo,

mi compañero, mi mejor amigo,

14a quien me unía una bella amistad,

con quien convivía en la casa de Dios.

15¡Que sorprenda la muerte a mis enemigos!

¡Que caigan vivos al sepulcro,

pues en ellos habita la maldad!

16Pero yo clamaré a Dios,

y el Señor me salvará.

17Mañana, tarde y noche

clamo angustiado, y él me escucha.

18Aunque son muchos los que me combaten,

él me rescata, me salva la vida

en la batalla que se libra contra mí.

19¡Dios, que reina para siempre,

habrá de oírme y los afligirá! Selah

Esa gente no cambia de conducta,

no tiene temor de Dios.

20Levantan la mano contra sus amigos

y no cumplen sus compromisos.

21Su boca es blanda como la manteca,

pero sus pensamientos son belicosos.

Sus palabras son más suaves que el aceite,

pero no son sino espadas desenvainadas.

22Encomienda al Señor tus afanes,

y él te sostendrá;

no permitirá que el justo caiga

y quede abatido para siempre.

23Tú, oh Dios, abatirás a los impíos

y los arrojarás en la fosa de la muerte;

la gente sanguinaria y mentirosa

no llegará ni a la mitad de su vida.

Yo, por mi parte, en ti confío.