Masalimo 55 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 55:1-23

Salimo 55

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe.

1Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu,

musakufulatire kupempha kwanga,

2mverani ndipo mundiyankhe.

Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru

3chifukwa cha mawu a adani anga,

chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa;

pakuti andidzetsera masautso

ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.

4Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga;

mantha a imfa andigwera.

5Mantha ndi kunjenjemera zandizinga;

mantha aakulu andithetsa nzeru.

6Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda!

Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.

7Ndikanathawira kutali

ndi kukakhala mʼchipululu.

8Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo;

kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”

9Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo;

pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.

10Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake;

nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.

11Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda;

kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.

12Akanakhala mdani akundinyoza, ine

ndikanapirira;

akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane,

ndikanakabisala.

13Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye,

bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.

14Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala

pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.

15Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi;

alowe mʼmanda ali amoyo

pakuti choyipa chili pakati pawo.

16Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu,

ndipo Yehova anandipulumutsa.

17Madzulo, mmawa ndi masana

ndimalira mowawidwa mtima,

ndipo Iye amamva mawu anga.

18Iye amandiwombola ine osavulazidwa

pa nkhondo imene yafika kulimbana nane,

ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.

19Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya,

adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga,

chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa

ndipo saopa Mulungu.

20Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake;

iye akuphwanya pangano ake.

21Mawu ake ndi osalala kuposa batala

komabe nkhondo ili mu mtima mwake;

mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta,

komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.

22Tulani nkhawa zanu kwa Yehova

ndipo Iye adzakulimbitsani;

Iye sadzalola kuti wolungama agwe.

23Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa

kulowa mʼdzenje lachiwonongeko;

anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo

sadzakhala moyo theka la masiku awo,

koma ine ndimadalira Inu.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Забур 55:1-14

Песнь 55

1Дирижёру хора. На мотив «О голубке в дальней дубраве». Мольба Давуда, когда филистимляне схватили его в Гате55:1 См. 1 Цар. 21:10-15; 27:1-4..

2Аллах, помилуй меня,

потому что люди меня затравили;

всякий день, нападая, меня теснят.

3Враг травит меня всякий день;

как же много воюющих со мной,

о Высочайший!55:3 Или: «тех, кто в гордыне со мной воюет».

4Когда мне страшно,

я на Тебя полагаюсь.

5На Аллаха, Чьё слово я славлю,

на Аллаха полагаюсь

и не устрашусь:

что может мне сделать смертный?

6А мои враги всякий день искажают слова мои,

всегда замышляют сделать мне зло.

7Они составляют заговоры, таятся,

наблюдают за каждым моим шагом,

желая меня убить.

8Так не дай им избежать наказания за их вину;

в гневе Своём, Аллах, низложи народы!

9У Тебя записаны все скитания мои;

собери мои слёзы в сосуд Свой –

не в Твоей ли книге они?

10И враги мои обратятся вспять,

когда я о помощи воззову.

Так я узнаю, что Аллах со мной.

11На Аллаха, Чьё слово я славлю,

на Вечного, Чьё слово я славлю,

12на Аллаха полагаюсь

и не устрашусь:

что может мне сделать человек?

13Аллах, я дам Тебе, что обещал;

я принесу Тебе жертвы благодарения.

14Ведь Ты спас меня от смерти

и не дал споткнуться моим ногам,

чтобы мне во свете живых

ходить пред Тобою.