Masalimo 53 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 53:1-6

Salimo 53

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide.

1Chitsiru chimati mu mtima mwake,

“Kulibe Mulungu.”

Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa;

palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.

2Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano

pa ana a anthu

kuti aone ngati alipo wina wanzeru,

wofunafuna Mulungu.

3Aliyense wabwerera,

iwo onse pamodzi akhala oyipa;

palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino,

ngakhale mmodzi.

4Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi;

anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi,

ndipo sapemphera kwa Mulungu?

5Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu

pamene panalibe kanthu kochititsa mantha.

Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo;

inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.

6Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni!

Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake,

lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!

Thai New Contemporary Bible

สดุดี 53:1-6

สดุดี 53

(สดด.14:1-7)

(ถึงหัวหน้านักร้อง ตามทำนองมาหะลัท มัสคิล53:0 หัวเรื่องสดุดี 53 คงจะเป็นศัพท์ทางวรรณกรรมหรือทางดนตรีของดาวิด)

1คนโง่รำพึงอยู่ในใจว่า

“ไม่มีพระเจ้า”

พวกเขาเสื่อมทรามและวิถีทางของพวกเขาก็ชั่วช้าสามานย์

ไม่มีสักคนที่ทำดี

2พระเจ้าทอดพระเนตรลงมาจากฟ้าสวรรค์

ดูมวลมนุษยชาติ

เพื่อดูว่ามีสักคนไหมที่เข้าใจ

มีสักคนไหมที่แสวงหาพระเจ้า

3ทุกคนได้หันหนีไปหมด

พวกเขากลายเป็นคนเสื่อมทรามไปด้วยกัน

ไม่มีสักคนที่ทำดี

ไม่มีแม้แต่คนเดียว

4พวกคนชั่วไม่รับรู้อะไรเลยหรือ?

พวกเขากลืนกินประชากรของเราดั่งอาหาร

พวกเขาไม่เคยร้องทูลพระเจ้า

5ดูสิ พวกเขาจมอยู่ในความตาย

ที่ซึ่งไม่มีอะไรน่าหวาดหวั่น

พระเจ้าทรงทำให้กระดูกของบรรดาผู้ที่โจมตีเจ้ากระจัดกระจาย

เจ้าจะทำให้พวกเขาอับอายขายหน้า เพราะพระเจ้าทรงรังเกียจพวกเขา

6ขอให้การช่วยกู้เพื่ออิสราเอลมาจากศิโยนเถิด!

เมื่อพระเจ้าทรงทำให้เหล่าประชากรของพระองค์กลับสู่สภาพดีดังเดิม

ให้ยาโคบชื่นชมยินดีและอิสราเอลเปรมปรีดิ์เถิด!