Masalimo 53 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 53:1-6

Salimo 53

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide.

1Chitsiru chimati mu mtima mwake,

“Kulibe Mulungu.”

Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa;

palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.

2Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano

pa ana a anthu

kuti aone ngati alipo wina wanzeru,

wofunafuna Mulungu.

3Aliyense wabwerera,

iwo onse pamodzi akhala oyipa;

palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino,

ngakhale mmodzi.

4Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi;

anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi,

ndipo sapemphera kwa Mulungu?

5Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu

pamene panalibe kanthu kochititsa mantha.

Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo;

inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.

6Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni!

Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake,

lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!

O Livro

Salmos 53:1-6

Salmo 53

Salmo didático de David, de acordo com Maalate53.0 Termo incerto que poderá estar ligado a uma melodia ou instrumento.. Para o diretor do coro.

1Diz o louco para consigo mesmo: “Deus não existe!”

Todos se têm corrompido e degenerado;

não há ninguém que faça o bem.

2Deus olha desde os céus para a humanidade,

para ver se existe alguém

que saiba conduzir-se com sabedoria

e busque Deus.

3Todos se desviaram e juntamente se corromperam;

não há quem faça o bem, absolutamente ninguém!

4Serão assim tão ignorantes, esses malfeitores,

que devoram o meu povo como se comessem pão,

que se recusam a chamar por Deus?

5Ali um terror dominou as suas vidas,

mas não havia nada a temer.

Deus espalhará os ossos desses que te cercavam;

estão condenados, porque Deus os rejeitou.

6Que bom seria se já tivesse vindo de Sião

a salvação do povo de Deus!

Que alegria será quando Deus libertar

os presos do seu povo e salvar Israel!