Masalimo 53 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 53:1-6

Salimo 53

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide.

1Chitsiru chimati mu mtima mwake,

“Kulibe Mulungu.”

Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa;

palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.

2Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano

pa ana a anthu

kuti aone ngati alipo wina wanzeru,

wofunafuna Mulungu.

3Aliyense wabwerera,

iwo onse pamodzi akhala oyipa;

palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino,

ngakhale mmodzi.

4Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi;

anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi,

ndipo sapemphera kwa Mulungu?

5Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu

pamene panalibe kanthu kochititsa mantha.

Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo;

inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.

6Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni!

Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake,

lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!

New Russian Translation

Псалтирь 53:1-9

Псалом 53

1Дирижеру хора. На струнных инструментах. Наставление Давида 2когда зифиты пришли и сказали Саулу: «У нас скрывается Давид»53:2 См. 1 Цар. 23:19-28; 26:1-2..

3Боже, спаси меня Своим именем;

оправдай меня Своей силой!

4Боже, услышь молитву мою;

внемли словам моих уст!

5Чужие восстали против меня,

беспощадные ищут жизни моей –

те, кто о Боге не думает. Пауза

6Но, воистину, Бог мне помощник;

Владыка меня укрепляет53:6 Так в некоторых древних переводах; букв.: «из тех, кто меня укрепляет» или «с теми, кто меня укрепляет»..

7Он воздаст врагам моим за зло,

погубит их ради Своей верности.

8Я добровольно принесу Тебе жертву.

Я буду славить имя Твое, Господь,

потому что оно прекрасно.

9Ведь Ты уберег меня от всех бед,

и я победно смотрел на врагов.