Masalimo 53 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 53:1-6

Salimo 53

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide.

1Chitsiru chimati mu mtima mwake,

“Kulibe Mulungu.”

Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa;

palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.

2Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano

pa ana a anthu

kuti aone ngati alipo wina wanzeru,

wofunafuna Mulungu.

3Aliyense wabwerera,

iwo onse pamodzi akhala oyipa;

palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino,

ngakhale mmodzi.

4Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi;

anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi,

ndipo sapemphera kwa Mulungu?

5Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu

pamene panalibe kanthu kochititsa mantha.

Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo;

inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.

6Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni!

Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake,

lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!