Masalimo 53 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 53:1-6

Salimo 53

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide.

1Chitsiru chimati mu mtima mwake,

“Kulibe Mulungu.”

Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa;

palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.

2Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano

pa ana a anthu

kuti aone ngati alipo wina wanzeru,

wofunafuna Mulungu.

3Aliyense wabwerera,

iwo onse pamodzi akhala oyipa;

palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino,

ngakhale mmodzi.

4Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi;

anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi,

ndipo sapemphera kwa Mulungu?

5Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu

pamene panalibe kanthu kochititsa mantha.

Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo;

inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.

6Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni!

Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake,

lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!

La Bible du Semeur

Psaumes 53:1-7

Egarement général53 Voir Ps 14.

1Au chef de chœur, méditation53.1 Signification incertaine. de David, à chanter avec accompagnement de flûtes53.1 Sens incertain..

2Les insensés pensent : ╵« Dieu n’existe pas. »

Ils sont corrompus, ╵ils commettent ╵des actes iniques ╵et abominables,

et aucun ne fait le bien53.2 Les v. 2-4 sont cités en Rm 3.10-12..

3Du haut du ciel, Dieu observe ╵tout le genre humain :

« Reste-t-il un homme sage

qui s’attend à Dieu ?

4Ils se sont tous fourvoyés, ╵tous sont corrompus,

et aucun ne fait le bien,

même pas un seul.

5Ceux qui font le mal ╵n’ont-ils rien compris ?

Car ils dévorent mon peuple, ╵tout comme on mange du pain53.5 Autres traductions : pour leur propre profit, ou ils mangent son pain. !

Jamais ils n’invoquent Dieu ! »

6Ils sont saisis d’épouvante,

quand il n’y a rien à craindre,

car Dieu disperse les os ╵de ceux qui t’attaquent,

tu les couvriras de honte, ╵car Dieu les a rejetés.

7Ah, que vienne du mont de Sion ╵le salut pour Israël !

Quand Dieu changera le sort ╵de son peuple,

Jacob criera d’allégresse, ╵Israël, de joie.