Masalimo 52 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 52:1-9

Salimo 52

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, ndakatulo ya Davide; pamene Doegi Mwedomu anapita kwa Sauli ndi kunena kuti “Davide wapita ku nyumba ya Ahimeleki.”

1Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira ndi zoyipa, iwe munthu wamphamvu?

Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira tsiku lonse,

iwe munthu wochititsa manyazi pamaso pa Mulungu?

2Tsiku lonse umakhalira kuganizira za kuwononga ena;

lilime lako lili ngati lumo lakuthwa,

ntchito yako nʼkunyenga.

3Iwe umakonda choyipa mʼmalo mwa kuyankhula choonadi.

Umakonda kunama kupambana kuyankhula zoona.

Sela

4Umakonda mawu onse opweteka,

iwe lilime lachinyengo!

5Zoonadi Mulungu adzakutsitsa kupita ku chiwonongeko chamuyaya:

iye adzakukwatula ndi kukuchotsa mʼtenti yako;

iye adzakuzula kuchoka mʼdziko la amoyo.

6Olungama adzaona zimenezi ndi kuchita mantha;

adzamuseka nʼkumanena kuti,

7“Pano tsopano pali munthu

amene sanayese Mulungu linga lake,

koma anakhulupirira chuma chake chambiri

nalimbika kuchita zoyipa!”

8Koma ine ndili ngati mtengo wa olivi

wobiriwira bwino mʼnyumba ya Mulungu;

ndimadalira chikondi chosatha cha Mulungu

kwa nthawi za nthawi.

9Ine ndidzakutamandani kwamuyaya chifukwa cha zimene mwachita;

chifukwa cha zimene mwachita; mʼdzina lanu ndidzayembekezera

pakuti dzina lanulo ndi labwino. Ndidzakutamandani pamaso pa oyera mtima anu.

King James Version

Psalms 52:1-9

To the chief Musician, Maschil, A Psalm of David, when Doeg the Edomite came and told Saul, and said unto him, David is come to the house of Ahimelech.

1Why boastest thou thyself in mischief, O mighty man? the goodness of God endureth continually.52.1 Maschil: or, of instruction

2Thy tongue deviseth mischiefs; like a sharp razor, working deceitfully.

3Thou lovest evil more than good; and lying rather than to speak righteousness. Selah.

4Thou lovest all devouring words, O thou deceitful tongue.52.4 O thou…: or, and the deceitful tongue

5God shall likewise destroy thee for ever, he shall take thee away, and pluck thee out of thy dwelling place, and root thee out of the land of the living. Selah.52.5 destroy…: Heb. beat thee down

6The righteous also shall see, and fear, and shall laugh at him:

7Lo, this is the man that made not God his strength; but trusted in the abundance of his riches, and strengthened himself in his wickedness.52.7 wickedness: or, substance

8But I am like a green olive tree in the house of God: I trust in the mercy of God for ever and ever.

9I will praise thee for ever, because thou hast done it: and I will wait on thy name; for it is good before thy saints.