Masalimo 52 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 52:1-9

Salimo 52

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, ndakatulo ya Davide; pamene Doegi Mwedomu anapita kwa Sauli ndi kunena kuti “Davide wapita ku nyumba ya Ahimeleki.”

1Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira ndi zoyipa, iwe munthu wamphamvu?

Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira tsiku lonse,

iwe munthu wochititsa manyazi pamaso pa Mulungu?

2Tsiku lonse umakhalira kuganizira za kuwononga ena;

lilime lako lili ngati lumo lakuthwa,

ntchito yako nʼkunyenga.

3Iwe umakonda choyipa mʼmalo mwa kuyankhula choonadi.

Umakonda kunama kupambana kuyankhula zoona.

Sela

4Umakonda mawu onse opweteka,

iwe lilime lachinyengo!

5Zoonadi Mulungu adzakutsitsa kupita ku chiwonongeko chamuyaya:

iye adzakukwatula ndi kukuchotsa mʼtenti yako;

iye adzakuzula kuchoka mʼdziko la amoyo.

6Olungama adzaona zimenezi ndi kuchita mantha;

adzamuseka nʼkumanena kuti,

7“Pano tsopano pali munthu

amene sanayese Mulungu linga lake,

koma anakhulupirira chuma chake chambiri

nalimbika kuchita zoyipa!”

8Koma ine ndili ngati mtengo wa olivi

wobiriwira bwino mʼnyumba ya Mulungu;

ndimadalira chikondi chosatha cha Mulungu

kwa nthawi za nthawi.

9Ine ndidzakutamandani kwamuyaya chifukwa cha zimene mwachita;

chifukwa cha zimene mwachita; mʼdzina lanu ndidzayembekezera

pakuti dzina lanulo ndi labwino. Ndidzakutamandani pamaso pa oyera mtima anu.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 52:1-11

Guds straf over en ond „helt”

1-2Til korlederen: En visdomssang af David, dengang Edomitten Doeg fortalte Saul, at David havde søgt hjælp hos Ahimelek.52,1-2 Se 1.Sam. 21–22, hvor Saul fik Doeg til at slå alle præsterne ihjel.

3Hvorfor prale af din ondskab, du stærke mand?

Gud er trofast, og han beskytter mig dag efter dag.

4Hele tiden lægger du onde planer.

Dine ord er dødbringende som skarpe knive.

5Du foretrækker ondt frem for godt,

løgn frem for sandhed.

6Du elsker at sige noget, som kan skade andre.

Hvor er du fuld af falskhed.

7Men Gud vil gøre det af med dig,

rive dig bort fra dit hjem,

rykke dig op fra de levendes land.

8Når de gudfrygtige ser det, vil de gyse,

de vil håne dig og sige:

9„Sådan går det dem,

der ikke regner med Gud,

men stoler på deres rigdom

og praler af deres ondskab.”

10Men jeg er som et frodigt oliventræ,

der trives i Herrens hus.

Jeg stoler altid på hans trofasthed og nåde.

11Herre, jeg vil takke dig for alt, hvad du gør for mig,

jeg vil forkynde din godhed i dine tjeneres nærvær.