Masalimo 51 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 51:1-19

Salimo 51

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba.

1Mundichitire chifundo, Inu Mulungu,

molingana ndi chikondi chanu chosasinthika;

molingana ndi chifundo chanu chachikulu

mufafanize mphulupulu zanga.

2Munditsuke zolakwa zanga zonse

ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.

3Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga,

ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.

4Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa

ndipo ndachita zoyipa pamaso panu,

Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama

pamene muyankhula ndi pamene muweruza.

5Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa,

wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.

6Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga;

mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.

7Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera,

munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala

8Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo,

mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.

9Mufulatire machimo anga

ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.

10Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu

ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.

11Musandichotse pamaso panu

kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.

12Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu

ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.

13Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu

kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.

14Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu,

Mulungu wa chipulumutso changa,

ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.

15Inu Ambuye tsekulani milomo yanga,

ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.

16Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba.

Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.

17Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka;

mtima wosweka ndi wachisoni

Inu Mulungu simudzawunyoza.

18Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere;

mumange makoma a Yerusalemu.

19Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo,

nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu;

ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.

New International Version

Psalms 51:1-19

Psalm 51In Hebrew texts 51:1-19 is numbered 51:3-21.

For the director of music. A psalm of David. When the prophet Nathan came to him after David had committed adultery with Bathsheba.

1Have mercy on me, O God,

according to your unfailing love;

according to your great compassion

blot out my transgressions.

2Wash away all my iniquity

and cleanse me from my sin.

3For I know my transgressions,

and my sin is always before me.

4Against you, you only, have I sinned

and done what is evil in your sight;

so you are right in your verdict

and justified when you judge.

5Surely I was sinful at birth,

sinful from the time my mother conceived me.

6Yet you desired faithfulness even in the womb;

you taught me wisdom in that secret place.

7Cleanse me with hyssop, and I will be clean;

wash me, and I will be whiter than snow.

8Let me hear joy and gladness;

let the bones you have crushed rejoice.

9Hide your face from my sins

and blot out all my iniquity.

10Create in me a pure heart, O God,

and renew a steadfast spirit within me.

11Do not cast me from your presence

or take your Holy Spirit from me.

12Restore to me the joy of your salvation

and grant me a willing spirit, to sustain me.

13Then I will teach transgressors your ways,

so that sinners will turn back to you.

14Deliver me from the guilt of bloodshed, O God,

you who are God my Savior,

and my tongue will sing of your righteousness.

15Open my lips, Lord,

and my mouth will declare your praise.

16You do not delight in sacrifice, or I would bring it;

you do not take pleasure in burnt offerings.

17My sacrifice, O God, is51:17 Or The sacrifices of God are a broken spirit;

a broken and contrite heart

you, God, will not despise.

18May it please you to prosper Zion,

to build up the walls of Jerusalem.

19Then you will delight in the sacrifices of the righteous,

in burnt offerings offered whole;

then bulls will be offered on your altar.