Masalimo 51 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 51:1-19

Salimo 51

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba.

1Mundichitire chifundo, Inu Mulungu,

molingana ndi chikondi chanu chosasinthika;

molingana ndi chifundo chanu chachikulu

mufafanize mphulupulu zanga.

2Munditsuke zolakwa zanga zonse

ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.

3Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga,

ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.

4Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa

ndipo ndachita zoyipa pamaso panu,

Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama

pamene muyankhula ndi pamene muweruza.

5Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa,

wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.

6Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga;

mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.

7Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera,

munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala

8Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo,

mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.

9Mufulatire machimo anga

ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.

10Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu

ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.

11Musandichotse pamaso panu

kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.

12Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu

ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.

13Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu

kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.

14Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu,

Mulungu wa chipulumutso changa,

ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.

15Inu Ambuye tsekulani milomo yanga,

ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.

16Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba.

Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.

17Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka;

mtima wosweka ndi wachisoni

Inu Mulungu simudzawunyoza.

18Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere;

mumange makoma a Yerusalemu.

19Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo,

nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu;

ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.

Luganda Contemporary Bible

Zabbuli 51:1-19

Zabbuli 51

Ya Mukulu wa Bayimbi. Zabbuli ya Dawudi. Nnabbi Nasani bwe yajja eri Dawudi, Dawudi ng’amaze okutwala Basuseba n’okutemula bba, Uliya.

151:1 a Bik 3:19 b Is 43:25; Bak 2:14Onsaasire, Ayi Mukama,

ggwe alina okwagala okutaggwaawo.

Olw’okusaasira kwo okungi

nziggyaako ebyonoono byange byonna.

251:2 a 1Yk 1:9 b Beb 9:14Nnaazaako obutali butuukirivu bwange,

ontukulize ddala okuva mu kibi kyange.

351:3 Is 59:12Ebyonoono byange mbikkiriza,

era ebibi byange mbimanyi bulijjo.

451:4 a Lub 20:6; Luk 15:21 b Bar 3:4*Ggwe wennyini ggwe nnyonoonye,

ne nkola ebitali bya butuukirivu mu maaso go ng’olaba;

noolwekyo by’oyogera bituufu,

era n’ensala yo ey’omusango ya bwenkanya.

551:5 Yob 14:4Ddala, nazaalibwa mu kibi;

kasookedde ntondebwa mu lubuto lwa mmange ndi mwonoonyi.

651:6 a Nge 2:6 b Zab 15:2Oyagala amazima agaviira ddala mu mutima gwange.

Ompe amagezi munda ddala mu nze.

751:7 a Lv 14:4; Beb 9:19 b Is 1:18Onnaaze n’ezobu51:7 Ezobu kimera ekisangibwa mu Asiya, era kikozesebwa okutuukiriza obulombolombo obw’enjawulo okutukuzibwa, mu Baebbulaniya ntukule

onnaaze ntukule n’okusinga omuzira.

851:8 Is 35:10Onzirize essanyu n’okwesiima,

amagumba gange ge wamenyaamenya gasanyuke.

951:9 Yer 16:17Totunuulira bibi byange,

era osangule ebyonoono byange byonna.

1051:10 a Zab 78:37; Bik 15:9 b Ez 18:31Ontondemu omutima omulongoofu, Ayi Katonda,

era onteekemu omwoyo omulungi munda yange.

1151:11 Bef 4:30Tongoba w’oli,

era tonzigyako Mwoyo wo Omutukuvu.

1251:12 Zab 13:5Onkomezeewo essanyu ery’obulokozi bwo,

era ompe omutima ogugondera by’oyagala,

1351:13 a Bik 9:21-22 b Zab 22:27ndyoke njigirizenga aboonoonyi amakubo go,

n’abakola ebibi bakukyukirenga bakomewo gy’oli.

1451:14 a 2Sa 12:9 b Zab 25:5 c Zab 35:28Ondokole mu kibi eky’okuyiwa omusaayi, Ayi Katonda,

ggwe Katonda ow’obulokozi bwange;

olulimi lwange lunaatenderezanga obutuukirivu bwo.

1551:15 Zab 9:14Ayi Mukama, yasamya emimwa gyange,

n’akamwa kange kanaakutenderezanga.

1651:16 1Sa 15:22; Zab 40:6Tosanyukira ssaddaaka, nandigikuleetedde;

n’ebiweebwayo ebyokebwa tobisanyukira.

1751:17 Zab 34:18Ssaddaaka Katonda gy’ayagala gwe mwoyo ogutegedde okusobya kwagwo.

Omutima ogumenyese era oguboneredde,

Ayi Katonda, toogugayenga.

1851:18 Zab 102:16; Is 51:3Okulaakulanye Sayuuni nga bw’osiima.

Yerusaalemi okizzeeko bbugwe waakyo.

1951:19 a Zab 4:5 b Zab 66:13 c Zab 66:15Olyoke osanyukire ssaddaaka ey’obutuukirivu,

ebiweebwayo ebyokebwa ebikusanyusa;

n’ente ziweebweyo ku kyoto kyo.