Masalimo 51 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 51:1-19

Salimo 51

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba.

1Mundichitire chifundo, Inu Mulungu,

molingana ndi chikondi chanu chosasinthika;

molingana ndi chifundo chanu chachikulu

mufafanize mphulupulu zanga.

2Munditsuke zolakwa zanga zonse

ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.

3Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga,

ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.

4Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa

ndipo ndachita zoyipa pamaso panu,

Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama

pamene muyankhula ndi pamene muweruza.

5Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa,

wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.

6Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga;

mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.

7Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera,

munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala

8Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo,

mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.

9Mufulatire machimo anga

ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.

10Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu

ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.

11Musandichotse pamaso panu

kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.

12Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu

ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.

13Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu

kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.

14Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu,

Mulungu wa chipulumutso changa,

ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.

15Inu Ambuye tsekulani milomo yanga,

ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.

16Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba.

Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.

17Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka;

mtima wosweka ndi wachisoni

Inu Mulungu simudzawunyoza.

18Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere;

mumange makoma a Yerusalemu.

19Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo,

nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu;

ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.

Hoffnung für Alle

Psalm 51:1-21

Herr, vergib mir!

1Ein Lied von David.

2Er schrieb es, nachdem der Prophet Nathan ihn wegen seines Ehebruchs mit Batseba zurechtgewiesen hatte.51,2 Vgl. 2. Samuel 12,1‒14.

3Du barmherziger Gott, sei mir gnädig!

Lösche meine Vergehen aus, denn du bist voll Erbarmen!

4Wasche meine ganze Schuld von mir ab

und reinige mich von meiner Sünde!

5Denn ich erkenne mein Unrecht,

meine Schuld steht mir ständig vor Augen.

6Gegen dich habe ich gesündigt – gegen dich allein!

Was du als böse ansiehst, das habe ich getan.

Darum bist du im Recht, wenn du mich verurteilst,

dein Richterspruch wird sich als wahr erweisen.

7Schon von Geburt an bestimmt die Sünde mein Leben;

ja, seit ich im Leib meiner Mutter entstand, liegt Schuld auf mir.

8Du freust dich, wenn ein Mensch von Herzen aufrichtig ist;

verhilf mir dazu und lass mich weise handeln!51,8 Wörtlich: Du willst Wahrheit im Innersten, und im Verborgenen wirst du mir Weisheit kundtun.

9Reinige mich von meiner Schuld,51,9 Wörtlich: Entsündige mich mit Ysop. – Vgl. »Ysop« in den Sacherklärungen. dann bin ich wirklich rein;

wasche meine Sünde ab, dann bin ich weißer als Schnee!

10Du hast mich hart bestraft; nun lass mich wieder Freude erfahren,

damit ich befreit aufatmen kann!

11Sieh nicht länger auf meine Schuld,

vergib mir alle meine Sünden!

12Erschaffe in mir ein reines Herz, o Gott;

erneuere mich und gib mir die Kraft, dir treu zu sein51,12 Wörtlich: gib mir einen neuen, gefestigten Geist.!

13Verstoße mich nicht aus deiner Nähe

und nimm deinen Heiligen Geist nicht von mir!

14Schenk mir wieder Freude über deine Rettung

und mach mich bereit, dir zu gehorchen!

15Dann will ich den Gottlosen deine Wege zeigen,

damit sie zu dir zurückkehren.

16Ich habe das Blut eines Menschen vergossen –

befreie mich von dieser Schuld, Gott, mein Retter!

Dann werde ich deine Gnade preisen und jubeln vor Freude.

17Herr, schenke mir die Worte,

um deine Größe zu rühmen!

18Du willst kein Schlachtopfer, sonst hätte ich es dir gebracht;

nein, Brandopfer gefallen dir nicht.

19Ich bin zerknirscht und verzweifelt über meine schwere Schuld.

Solch ein Opfer gefällt dir, o Gott, du wirst es nicht ablehnen.

20Zeige Zion deine Liebe

und festige die Mauern Jerusalems!

21Dann werden dir unsere Opfer wieder gefallen,

die wir mit aufrichtigem Herzen darbringen.

Dann werden wir wieder Stiere schlachten

und sie zu deiner Ehre auf dem Altar verbrennen.