Masalimo 50 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 50:1-23

Salimo 50

Salimo la Asafu.

1Wamphamvuyo, Yehova Mulungu,

akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi

kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.

2Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri

Mulungu akuwala.

3Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete;

moto ukunyeketsa patsogolo pake,

ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho

4Iye akuyitanitsa zamumlengalenga

ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.

5Mundisonkhanitsire okhulupirika anga,

amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.

6Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake,

pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.

7Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula,

iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa;

ndine Mulungu, Mulungu wako.

8Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako,

kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.

9Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako

kapena mbuzi za mʼkhola lako,

10pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga

ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.

11Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri

ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.

12Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani,

pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.

13Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna

kapena kumwa magazi a mbuzi?

14“Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu,

kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.

15Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso;

Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”

16Koma kwa woyipa, Mulungu akuti,

“Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga

kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?

17Iwe umadana ndi malangizo anga

ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.

18Ukaona wakuba umamutsatira,

umachita maere ako pamodzi ndi achigololo

19Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa

ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.

20Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako

ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.

21Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete;

umaganiza kuti ndine wofanana nawe

koma ndidzakudzudzula

ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.

22“Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu

kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:

23Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza,

ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse

chipulumutso cha Mulungu.”

La Bible du Semeur

Psaumes 50:1-23

Dieu va juger son peuple

1Psaume d’Asaph50.1 Sur Asaph, voir 1 Ch 6.16-17, 24 ; 25.1 ; 2 Ch 35.15. Asaph était l’un des trois chefs de chœur de David ; il nous a laissé douze psaumes..

Le Dieu suprême, ╵l’Eternel a parlé ╵et il a convoqué la terre

du levant du soleil ╵à son couchant.

2De Sion, parfaite en beauté,

Dieu resplendit.

3Qu’il vienne notre Dieu ! ╵Qu’il ne garde pas le silence !

Devant lui, un feu dévorant,

autour de lui, c’est l’ouragan.

4Le ciel en haut, il le convoque,

et il convoque aussi la terre : ╵il vient pour gouverner son peuple.

5« Rassemblez ceux qui me sont attachés,

ceux qui ont conclu avec moi ╵l’alliance par le sacrifice. »

6Le ciel publiera sa justice,

c’est Dieu qui gouverne le monde.

Pause

7Mon peuple, écoute, je te parle,

Israël, je témoigne contre toi,

moi qui suis Dieu, ton Dieu.

8Ce n’est pas pour tes sacrifices ╵que je t’adresse des reproches :

j’ai constamment ╵tes holocaustes sous les yeux.

9Je ne prendrai ╵ni des taureaux dans ton étable,

ni des boucs dans tes fermes,

10car tous les animaux ╵des forêts sont à moi,

à moi, les bêtes par milliers ╵dans les montagnes !

11Je connais tous les oiseaux des montagnes

et tous les animaux des champs ╵me sont à portée de la main.

12Si j’avais faim, te le dirais-je ?

L’univers est à moi ╵et tout ce qu’il renferme.

13Vais-je manger ╵la viande des taureaux,

ou m’abreuver ╵du sang des boucs ?

14En sacrifice à Dieu ╵offre donc ta reconnaissance !

Accomplis envers le Très-Haut ╵les vœux que tu as faits.

15Alors tu pourras m’appeler ╵au jour de la détresse :

je te délivrerai, ╵et tu me rendras gloire.

16Au méchant aussi, Dieu s’adresse :

« Pourquoi rabâches-tu mes lois ?

Tu as mon alliance à la bouche,

17mais tu détestes l’instruction

et tu rejettes mes paroles ╵au loin, derrière toi.

18A peine as-tu vu un voleur, ╵tu deviens son complice,

et puis, tu fais cause commune ╵avec les adultères.

19Ta bouche forge la malice.

Ta langue tisse le mensonge.

20Lorsque tu t’assieds avec d’autres, ╵tu calomnies ton frère,

et tu jettes le déshonneur ╵sur le fils de ta mère.

21Lorsque tu agissais ainsi ╵et que je n’ai rien dit,

as-tu vraiment imaginé ╵que je te ressemblais ?

Aussi je vais te corriger, ╵tout mettre sous tes yeux.

22Comprenez donc cela, ╵vous qui ignorez Dieu,

sinon je vous déchirerai ╵et nul ne vous délivrera.

23Qui, en guise de sacrifice, ╵m’offre de la reconnaissance, ╵celui-là me rend gloire,

et à celui qui règle son chemin,

je ferai voir ╵le salut que Dieu donne. »