Masalimo 5 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 5:1-12

Salimo 5

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe zoyimbira za zitoliro. Salimo la Davide.

1Tcherani khutu ku mawu anga, Inu Yehova,

ganizirani za kusisima kwanga

2Mverani kulira kwanga kofuna thandizo,

Mfumu yanga ndi Mulungu wanga,

pakuti kwa Inu, ine ndikupemphera.

3Mmawa, Yehova mumamva mawu anga;

Mmawa ndimayala zopempha zanga pamaso panu

ndi kudikira mwachiyembekezo.

4Inu si Mulungu amene mumasangalala ndi zoyipa;

choyipa sichikhala pamaso panu.

5Onyada sangathe kuyima pamaso panu;

Inu mumadana ndi onse ochita zoyipa.

6Mumawononga iwo amene amanena mabodza;

anthu akupha ndi achinyengo,

Yehova amanyansidwa nawo.

7Koma Ine, mwa chifundo chanu chachikulu,

ndidzalowa mʼNyumba yanu;

mwa ulemu ndidzaweramira pansi

kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera.

8Tsogolereni Inu Yehova, mwa chilungamo chanu

chifukwa cha adani anga ndipo

wongolani njira yanu pamaso panga.

9Palibe mawu ochokera mʼkamwa mwawo amene angadalirike;

mtima wawo wadzaza ndi chiwonongeko.

Kummero kwawo kuli ngati manda apululu;

ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.

10Lengezani kuti ndi olakwa, Inu Mulungu!

Zochita zawo zoyipa zikhale kugwa kwawo.

Achotseni pamaso panu chifukwa cha machimo awo ambiri,

pakuti awukira Inu.

11Koma lolani kuti onse amene apeza chitetezo mwa Inu akondwere;

lolani kuti aziyimba nthawi zonse chifukwa cha chimwemwe.

Aphimbeni ndi chitetezo chanu,

iwo amene amakonda dzina lanu akondwere mwa Inu.

12Ndithu, Inu Yehova, mumadalitsa olungama;

mumawazungulira ndi kukoma mtima kwanu ngati chishango.

Korean Living Bible

시편 5:1-12

보호의 기도

(다윗의 시. 성가대 지휘자를 따라 관악기에 맞춰 부른 노래)

1여호와여, 내 말에

귀를 기울이시고

나의 5:1 또는 ‘심사를’탄식을 생각하소서.

2나의 왕, 나의 하나님이시여,

나의 부르짖는 소리를 들으소서.

내가 주께 기도합니다.

3여호와여, 주는 아침마다

내 소리를 들으실 것입니다.

내가 주께 기도하며

간절한 마음으로

주의 응답을 기다리겠습니다.

4주는 악을

기뻐하는 신이 아니시므로

악한 자가

주와 함께할 수 없습니다.

5교만한 자가

주 앞에 설 수 없는 것은

주께서 악을 행하는 자를

모두 미워하시기 때문입니다.

6주께서는

거짓말하는 자를 멸하시고

살인자와 사기꾼을

아주 싫어하십니다.

7그러나 내가

주의 크신 사랑을 입었으므로

주의 거룩한 성전에 들어가

주께 경배하겠습니다.

8여호와여, 나에게는

많은 원수들이 있습니다.

나를 인도하셔서

주의 뜻을 행하게 하시고

주의 길을 밝히셔서

내가 따르게 하소서.

9내 원수들의 말은

하나도 믿을 수가 없습니다.

그들의 마음은

악으로 가득 차 있고

그들의 목구멍은

열린 무덤 같으며

그들의 혀로는

아첨하고 있습니다.

10하나님이시여,

그들을 죄인으로 단정하시고

그들로 자기 꾀에 빠지게 하소서.

그들이 죄가 많으니

그들을 추방하소서.

그들이 주를 거역하였습니다.

11그러나 5:11 또는 ‘주에게 피하는 자는’주를 신뢰하는 자는

기뻐할 것입니다.

주를 사랑하는 자들을 보호하셔서

그들이 주 안에서

기뻐 외치게 하소서.

12주는 의로운 자에게 복을 주시고

사랑의 방패로

저들을 지키십니다.