Masalimo 5 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 5:1-12

Salimo 5

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe zoyimbira za zitoliro. Salimo la Davide.

1Tcherani khutu ku mawu anga, Inu Yehova,

ganizirani za kusisima kwanga

2Mverani kulira kwanga kofuna thandizo,

Mfumu yanga ndi Mulungu wanga,

pakuti kwa Inu, ine ndikupemphera.

3Mmawa, Yehova mumamva mawu anga;

Mmawa ndimayala zopempha zanga pamaso panu

ndi kudikira mwachiyembekezo.

4Inu si Mulungu amene mumasangalala ndi zoyipa;

choyipa sichikhala pamaso panu.

5Onyada sangathe kuyima pamaso panu;

Inu mumadana ndi onse ochita zoyipa.

6Mumawononga iwo amene amanena mabodza;

anthu akupha ndi achinyengo,

Yehova amanyansidwa nawo.

7Koma Ine, mwa chifundo chanu chachikulu,

ndidzalowa mʼNyumba yanu;

mwa ulemu ndidzaweramira pansi

kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera.

8Tsogolereni Inu Yehova, mwa chilungamo chanu

chifukwa cha adani anga ndipo

wongolani njira yanu pamaso panga.

9Palibe mawu ochokera mʼkamwa mwawo amene angadalirike;

mtima wawo wadzaza ndi chiwonongeko.

Kummero kwawo kuli ngati manda apululu;

ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.

10Lengezani kuti ndi olakwa, Inu Mulungu!

Zochita zawo zoyipa zikhale kugwa kwawo.

Achotseni pamaso panu chifukwa cha machimo awo ambiri,

pakuti awukira Inu.

11Koma lolani kuti onse amene apeza chitetezo mwa Inu akondwere;

lolani kuti aziyimba nthawi zonse chifukwa cha chimwemwe.

Aphimbeni ndi chitetezo chanu,

iwo amene amakonda dzina lanu akondwere mwa Inu.

12Ndithu, Inu Yehova, mumadalitsa olungama;

mumawazungulira ndi kukoma mtima kwanu ngati chishango.

Het Boek

Psalmen 5:1-13

1Een psalm van David voor de koordirigent. Te begeleiden met fluitspel.

2O Here, wilt U mijn gebed aanhoren?

Luister toch naar mijn smeken.

3God, U bent mijn Koning

en ik richt mij tot U.

4Elke morgen kijk ik omhoog naar U

en wacht op uw antwoord,

en U hoort mij roepen.

5Ik weet dat slechtheid

bij U geen standhoudt

en dat geen enkele goddeloze

op uw bescherming kan rekenen.

6Hoogmoedige zondaars

kunnen uw onderzoekende blik niet doorstaan,

omdat U hun slechte daden haat.

7Om hun leugens zult U hen vernietigen,

U verafschuwt moord en bedrog, Here.

8Ik zelf mag dankzij uw genade en liefde

uw tempel binnengaan.

Met diep ontzag zal ik U eren.

9Here, wilt U mij leiden?

Anders zullen mijn vijanden over mij zegevieren.

Wilt U mij duidelijk maken wat ik moet doen

en welke weg ik moet inslaan?

10Mijn tegenstanders zullen elke kans aangrijpen

om mij in een kwaad daglicht te stellen.

Wat uit hun mond komt,

stinkt naar zonde en dood,

zij gebruiken hun tong voor leugen en bedrog.

Hun lippen spuwen dodelijk vergif.

11O God, spreek het ‘schuldig’ over hen uit!

Vang hen met hun eigen valstrikken,

verdrijf hen om de overvloed van hun overtredingen,

want zij komen in opstand tegen U.

12Maar ieder die zijn vertrouwen op U stelt,

zal zich verheugen.

Zij zullen tot in eeuwigheid van vreugde juichen,

omdat U hen beschermt.

Dan zal ieder die U liefheeft,

overlopen van blijdschap.

13Want U, Here, zegent uw volgelingen.

U beschermt hen met uw schild van liefde.