Masalimo 5 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 5:1-12

Salimo 5

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe zoyimbira za zitoliro. Salimo la Davide.

1Tcherani khutu ku mawu anga, Inu Yehova,

ganizirani za kusisima kwanga

2Mverani kulira kwanga kofuna thandizo,

Mfumu yanga ndi Mulungu wanga,

pakuti kwa Inu, ine ndikupemphera.

3Mmawa, Yehova mumamva mawu anga;

Mmawa ndimayala zopempha zanga pamaso panu

ndi kudikira mwachiyembekezo.

4Inu si Mulungu amene mumasangalala ndi zoyipa;

choyipa sichikhala pamaso panu.

5Onyada sangathe kuyima pamaso panu;

Inu mumadana ndi onse ochita zoyipa.

6Mumawononga iwo amene amanena mabodza;

anthu akupha ndi achinyengo,

Yehova amanyansidwa nawo.

7Koma Ine, mwa chifundo chanu chachikulu,

ndidzalowa mʼNyumba yanu;

mwa ulemu ndidzaweramira pansi

kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera.

8Tsogolereni Inu Yehova, mwa chilungamo chanu

chifukwa cha adani anga ndipo

wongolani njira yanu pamaso panga.

9Palibe mawu ochokera mʼkamwa mwawo amene angadalirike;

mtima wawo wadzaza ndi chiwonongeko.

Kummero kwawo kuli ngati manda apululu;

ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.

10Lengezani kuti ndi olakwa, Inu Mulungu!

Zochita zawo zoyipa zikhale kugwa kwawo.

Achotseni pamaso panu chifukwa cha machimo awo ambiri,

pakuti awukira Inu.

11Koma lolani kuti onse amene apeza chitetezo mwa Inu akondwere;

lolani kuti aziyimba nthawi zonse chifukwa cha chimwemwe.

Aphimbeni ndi chitetezo chanu,

iwo amene amakonda dzina lanu akondwere mwa Inu.

12Ndithu, Inu Yehova, mumadalitsa olungama;

mumawazungulira ndi kukoma mtima kwanu ngati chishango.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 5:1-12

Salmo 5

Al director musical. Acompáñese con flautas. Salmo de David.

1Atiende, Señor, a mis palabras;

toma en cuenta mis gemidos.

2Escucha mis súplicas, rey mío y Dios mío,

porque a ti elevo mi plegaria.

3Por la mañana, Señor, escuchas mi clamor;

por la mañana te presento mis ruegos,

y quedo esperando tu respuesta.

4Tú no eres un Dios que se complazca en lo malo;

a tu lado no tienen cabida los malvados.

5No hay lugar en tu presencia para los altivos,

pues aborreces a todos los malhechores.

6Tú destruyes a los mentirosos

y aborreces a los tramposos y asesinos.

7Pero yo, por tu gran amor

puedo entrar en tu casa;

puedo postrarme reverente

hacia tu santo templo.

8Señor, por causa de mis enemigos,

dirígeme en tu justicia;

endereza delante de mí tu senda.

9En sus palabras no hay sinceridad;

en su interior solo hay corrupción.

Su garganta es un sepulcro abierto;

con su lengua profieren engaños.

10¡Condénalos, oh Dios!

¡Que caigan por sus propias intrigas!

¡Recházalos por la multitud de sus crímenes,

porque se han rebelado contra ti!

11Pero que se alegren todos los que en ti buscan refugio;

¡que canten siempre jubilosos!

Extiéndeles tu protección, y que en ti se regocijen

todos los que aman tu nombre.

12Porque tú, Señor, bendices a los justos;

cual escudo los rodeas con tu buena voluntad.