Masalimo 5 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 5:1-12

Salimo 5

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe zoyimbira za zitoliro. Salimo la Davide.

1Tcherani khutu ku mawu anga, Inu Yehova,

ganizirani za kusisima kwanga

2Mverani kulira kwanga kofuna thandizo,

Mfumu yanga ndi Mulungu wanga,

pakuti kwa Inu, ine ndikupemphera.

3Mmawa, Yehova mumamva mawu anga;

Mmawa ndimayala zopempha zanga pamaso panu

ndi kudikira mwachiyembekezo.

4Inu si Mulungu amene mumasangalala ndi zoyipa;

choyipa sichikhala pamaso panu.

5Onyada sangathe kuyima pamaso panu;

Inu mumadana ndi onse ochita zoyipa.

6Mumawononga iwo amene amanena mabodza;

anthu akupha ndi achinyengo,

Yehova amanyansidwa nawo.

7Koma Ine, mwa chifundo chanu chachikulu,

ndidzalowa mʼNyumba yanu;

mwa ulemu ndidzaweramira pansi

kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera.

8Tsogolereni Inu Yehova, mwa chilungamo chanu

chifukwa cha adani anga ndipo

wongolani njira yanu pamaso panga.

9Palibe mawu ochokera mʼkamwa mwawo amene angadalirike;

mtima wawo wadzaza ndi chiwonongeko.

Kummero kwawo kuli ngati manda apululu;

ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.

10Lengezani kuti ndi olakwa, Inu Mulungu!

Zochita zawo zoyipa zikhale kugwa kwawo.

Achotseni pamaso panu chifukwa cha machimo awo ambiri,

pakuti awukira Inu.

11Koma lolani kuti onse amene apeza chitetezo mwa Inu akondwere;

lolani kuti aziyimba nthawi zonse chifukwa cha chimwemwe.

Aphimbeni ndi chitetezo chanu,

iwo amene amakonda dzina lanu akondwere mwa Inu.

12Ndithu, Inu Yehova, mumadalitsa olungama;

mumawazungulira ndi kukoma mtima kwanu ngati chishango.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 5:1-13

Beskyttet under Herrens nåde

1Til korlederen: Brug fløjterne. En sang af David.

2Herre, hør min bøn,

lyt til mine dybe suk.

3Min Konge og min Gud, hør mit råb om hjælp,

for til dig vil jeg klage min nød.

4Om morgenen løfter jeg min røst til dig,

jeg lægger min sag frem for dig og venter.

5Gud, du hader grusomheder

og kan ikke acceptere ondskab.

6Oprørere får ikke adgang til dig,

for du hader de onde.

7Du tilintetgør dem, der lyver,

du afskyr vold og bedrageri.

8Men jeg kan gå ind i dit tempel

på grund af din trofaste nåde

og tilbede dig i ærefrygt.

9Herre, led mig ad den rette vej,

så mine fjender ikke fælder mig.

Vis mig den vej, jeg skal gå,

og fortæl mig, hvad jeg skal gøre.

10Mine fjender lyver konstant,

de er kun ude på at gøre fortræd.

Deres strube stinker som en åben grav,

deres tunge er belagt med smiger.

11Drag dem til ansvar, oh, Gud,

fang dem i deres egne fælder.

Straf dem for deres trodsighed,

for det er dig, de gør oprør imod.

12Men lad alle, som stoler på dig, juble.

Lad dem råbe af fryd til hver en tid.

Du beskytter dem, der følger dig trofast,

så de altid er fyldt med glæde.

13Du velsigner jo de gudfrygtige, Herre,

dækker dem med din nådes skjold.