Masalimo 49 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 49:1-20

Salimo 49

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora.

1Imvani izi anthu a mitundu yonse;

mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,

2anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika,

olemera pamodzinso ndi osauka:

3Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru;

mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.

4Ndidzatchera khutu langa ku mwambo,

ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.

5Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika,

pamene achinyengo oyipa andizungulira.

6Iwo amene adalira kulemera kwawo

ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?

7Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake

kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.

8Dipo la moyo ndi la mtengowapatali,

palibe malipiro amene angakwanire,

9kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya

ndi kusapita ku manda.

10Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira;

opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka

ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.

11Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya,

malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo,

ngakhale anatchula malo mayina awo.

12Ngakhale munthu akhale wachuma chotani,

adzafa ngati nyama.

13Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha,

ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula.

Sela

14Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda,

ndipo imfa idzawadya.

Olungama adzawalamulira mmawa;

matupi awo adzavunda mʼmanda,

kutali ndi nyumba zawo zaufumu.

15Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda;

ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini.

16Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera,

pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;

17Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira,

ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.

18Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala,

ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,

19iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake,

amene sadzaonanso kuwala.

20Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru

adzafa ngati nyama yakuthengo.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 49:1-21

Rigdom set i dødens perspektiv

1Til korlederen: En sang af Koras slægt.

2Hør her, alle folkeslag,

lyt til mig, alle folk på jorden,

3høj og lav, rig og fattig.

4Jeg taler med visdom,

og mine tanker er fulde af indsigt.

5Jeg har lyttet til mange ordsprog

og giver min indsigt videre med sang og musik.

6Jeg har intet at frygte i vanskelige tider,

selv om bedragere omringer mig på alle sider.

7De stoler på deres rigdom,

praler af alt det, de ejer.

8Men ingen kan betale sig fra at skulle dø,

for Gud bestemmer, hvornår livet er slut.

9Gud har sat prisen så højt,

at den slags aldrig kan lade sig gøre.

10Ellers kunne den rige jo leve evigt

og aldrig opleve død og grav.

11Alle ved, at selv vise folk dør.

De ender i graven akkurat som tåberne

og efterlader deres rigdom til andre.

12Selv om de er kendt og ejer både gods og guld,

bliver graven deres hjem til slut,

og de vender aldrig tilbage derfra.

13Selv de rige lever ikke evigt.

De dør ligesom dyrene og forsvinder.

14Sådan går det med de selvsikre,

dem, der tror, de kan klare alt.

15Som får bliver de gennet ned i dødsriget.

Det er døden, der driver dem af sted.

Næste morgen går mennesker hen over deres grav,

mens de selv rådner op i deres nye bolig.

16Men Gud har magt til at redde mit liv,

han kan rive mig ud af dødens kløer.

17Derfor skal du ikke blive modløs,

hvis nogle bliver styrtende rige,

18for i døden tager de intet med sig,

deres velstand må de lade tilbage.

19Om end de er selvsikre hele livet,

og folk berømmer dem for deres succes,

20så ender de dog hos deres forfædre

og ser aldrig dagens lys igen.

21De, der stoler på deres rigdom, er uden forstand,

for det går dem som dyrene, de skal alle dø.