Masalimo 48 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 48:1-14

Salimo 48

Nyimbo. Salimo la ana a Kora.

1Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando

mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.

2Lokongola mu utali mwake,

chimwemwe cha dziko lonse lapansi.

Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni,

mzinda wa Mfumu yayikulu.

3Mulungu ali mu malinga ake;

Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.

4Pamene mafumu anasonkhana pamodzi,

pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,

5iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri;

anathawa ndi mantha aakulu.

6Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera,

ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.

7Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi

zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.

8Monga momwe tinamvera,

kotero ife tinaona

mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse,

mu mzinda wa Mulungu wathu.

Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.

9Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu,

ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.

10Monga dzina lanu, Inu Mulungu,

matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi

dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.

11Phiri la Ziyoni likukondwera,

midzi ya Yuda ndi yosangalala

chifukwa cha maweruzo anu.

12Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo,

werengani nsanja zake.

13Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake,

penyetsetsani malinga ake,

kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.

14Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha;

Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.