Masalimo 47 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 47:1-9

Salimo 47

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora.

1Ombani mʼmanja, inu anthu onse;

fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.

2Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba;

Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!

3Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu;

anayika anthu pansi pa mapazi athu.

4Iye anatisankhira cholowa chathu,

chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda.

Sela

5Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe,

Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.

6Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando;

imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.

7Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi;

imbirani Iye salimo la matamando.

8Mulungu akulamulira mitundu ya anthu;

Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.

9Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana

monga anthu a Mulungu wa Abrahamu,

pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu;

Iye wakwezedwa kwakukulu.

Korean Living Bible

시편 47:1-9

세상의 왕이신 하나님

(고라 자손의 시. 성가대 지휘자를 따라 부른 노래)

1너희 모든 백성들아,

손뼉을 치며

즐거운 소리로 하나님께 외쳐라.

2가장 높으신 여호와는

두려워해야 할 분이시니

그는 온 세상을 다스리는

위대한 왕이심이라.

3여호와께서 세계 만민을

우리 발 아래 복종하게 하시고

4우리가 살 땅을 택하셨으니

47:4 또는 ‘사랑하신 야곱의 영화로다’사랑하는 자기 백성의

자랑스런 유산이라네.

5하나님이 기쁨의 함성과

나팔 소리 가운데

47:5 암시됨.자기 보좌로 올라가신다.

6찬양하라. 하나님을 찬양하라.

찬양하라. 우리의 왕을 찬양하라.

7하나님은

온 세계를 다스리는 왕이시다.

노래로 그를 찬양하라.

8하나님이

거룩한 보좌에 앉아

온 세상을 다스리신다.

9이방 나라 통치자들이 모여서

아브라함의 하나님의

백성이 되는구나.

세상의 모든 47:9 또는 ‘방패는’왕들이

하나님께 속했으니

그가 크게 높임을 받는구나.