Masalimo 47 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 47:1-9

Salimo 47

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora.

1Ombani mʼmanja, inu anthu onse;

fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.

2Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba;

Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!

3Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu;

anayika anthu pansi pa mapazi athu.

4Iye anatisankhira cholowa chathu,

chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda.

Sela

5Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe,

Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.

6Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando;

imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.

7Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi;

imbirani Iye salimo la matamando.

8Mulungu akulamulira mitundu ya anthu;

Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.

9Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana

monga anthu a Mulungu wa Abrahamu,

pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu;

Iye wakwezedwa kwakukulu.

Het Boek

Psalmen 47:1-10

1Een psalm van de Korachieten voor de koordirigent.

2Klap in uw handen, alle volken op aarde,

juich voor God met lofliederen.

3De Here, de Allerhoogste, is beroemd en gevreesd,

Hij is de grote Koning van de hele aarde.

4Hij laat ons andere volken overwinnen,

wij heersen over andere landen.

5Hij zoekt voor ons een erfdeel uit,

waar Jakob trots op zal zijn.

God houdt van Jakob.

6God stijgt ten hemel

onder juichende klanken,

de Here stijgt ten hemel

bij het geluid van schallende trompetten.

7Zing voor God, zing psalmen voor onze Koning,

laten onze lofliederen voor Hem opklinken.

8God is immers Koning over de hele aarde!

Zing voor Hem een psalm, een prachtig lied.

9God regeert vanaf zijn heilige troon

over alle volken op aarde.

10De leiders van alle volken komen bij elkaar

en sluiten zich aan bij het volk van Abrahams God.

Want alle bescherming die de aarde biedt,

is van God.

Hij is de Allerhoogste.