Masalimo 46 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 46:1-11

Salimo 46

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Nyimbo ya anamwali.

1Mulungu ndiye kothawira kwathu ndi mphamvu yathu,

thandizo lopezekeratu pa nthawi ya mavuto.

2Nʼchifukwa chake sitidzaopa ngakhale dziko lapansi lisunthike,

ngakhale mapiri agwe pakati pa nyanja,

3ngakhale madzi ake atakokoma ndi kuchita thovu,

ngakhale mapiri agwedezeke ndi kukokoma kwake.

4Kuli mtsinje umene njira zake za madzi zimasangalatsa mzinda wa Mulungu,

malo oyera kumene Wammwambamwamba amakhalako.

5Mulungu ali mʼkati mwake, iwo sudzagwa;

Mulungu adzawuthandiza mmawa.

6Mitundu ikupokosera, mafumu akugwa;

Iye wakweza mawu ake, dziko lapansi likusungunuka.

7Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife,

Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.

8Bwerani kuti mudzaone ntchito za Yehova,

chiwonongeko chimene wachibweretsa pa dziko lapansi.

9Iye amathetsa nkhondo ku malekezero a dziko lapansi;

Iye amathyola uta ndi kupindapinda mkondo;

amatentha zishango ndi moto.

10Iye akuti, “Khala chete, ndipo dziwa kuti ndine Mulungu;

ndidzakwezedwa pakati pa mitundu ya anthu;

ine ndidzakwezedwa mʼdziko lapansi.”

11Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife,

Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.

New Serbian Translation

Псалми 46:1-11

Псалам 46

Хоровођи. За потомке Корејеве. Песма за високе гласове.

1Бог нам је уточиште и сила,

трајни помоћник у невољи.

2Не бојмо се, зато, кад се земља љуља,

кад се горе руше у дубине мора.

3Ма, нек буче и пене се његове воде,

нек се горе тресу од његове силе. Села

4Тече река и њене притоке,

граду Божијем радост доносе,

светом месту где Свевишњи живи.

5Бог је усред њега, помаћи се неће,

Бог ће му помоћи у сам освит јутра.

6Буне се народи, пропадају царства,

кад глас повиси земља се раствара.

7С нама је Господ над војскама,

Бог Јаковљев наша је тврђава. Села

8Дођите, размотрите дела Господња,

који пустош по земљи оставља.

9Он прекида ратове до на крај земље,

лук крши, копље прелама,

бојна кола огњу изручује.

10Утихните и знајте да сам ја Бог,

узвишен међу народима,

узвишен на земљи.

11С нама је Господ над војскама,

Бог Јаковљев наша је тврђава. Села