Masalimo 46 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 46:1-11

Salimo 46

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Nyimbo ya anamwali.

1Mulungu ndiye kothawira kwathu ndi mphamvu yathu,

thandizo lopezekeratu pa nthawi ya mavuto.

2Nʼchifukwa chake sitidzaopa ngakhale dziko lapansi lisunthike,

ngakhale mapiri agwe pakati pa nyanja,

3ngakhale madzi ake atakokoma ndi kuchita thovu,

ngakhale mapiri agwedezeke ndi kukokoma kwake.

4Kuli mtsinje umene njira zake za madzi zimasangalatsa mzinda wa Mulungu,

malo oyera kumene Wammwambamwamba amakhalako.

5Mulungu ali mʼkati mwake, iwo sudzagwa;

Mulungu adzawuthandiza mmawa.

6Mitundu ikupokosera, mafumu akugwa;

Iye wakweza mawu ake, dziko lapansi likusungunuka.

7Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife,

Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.

8Bwerani kuti mudzaone ntchito za Yehova,

chiwonongeko chimene wachibweretsa pa dziko lapansi.

9Iye amathetsa nkhondo ku malekezero a dziko lapansi;

Iye amathyola uta ndi kupindapinda mkondo;

amatentha zishango ndi moto.

10Iye akuti, “Khala chete, ndipo dziwa kuti ndine Mulungu;

ndidzakwezedwa pakati pa mitundu ya anthu;

ine ndidzakwezedwa mʼdziko lapansi.”

11Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife,

Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Забур 46:1-10

Песнь 46

1Дирижёру хора. Песнь потомков Кораха.

2Рукоплещите, все народы,

вознесите Аллаху крик радости.

3Как грозен Вечный, Высочайший,

великий Царь над всей землёй!

4Он покорил нам народы,

ногами мы попираем племена.

5Он избрал нам наследие –

гордость Якуба, которого Он возлюбил. Пауза

6Аллах вознёсся под крики радости;

Вечный вознёсся под звуки рогов.

7Пойте Аллаху хвалу, пойте!

Пойте хвалу нашему Царю, пойте!

8Аллах – Царь над всей землёй;

пойте Ему искусную песнь.

9Аллах царит над народами;

Аллах восседает на святом престоле Своём.

10Собираются вожди народов

вместе с народом Бога Ибрахима,

ведь земные правители46:10 Букв.: «щиты». принадлежат Аллаху;

Он высоко превознесён над ними.